< 以赛亚书 38 >

1 那时希西家病得要死,亚摩斯的儿子先知以赛亚去见他,对他说:“耶和华如此说:你当留遗命与你的家,因为你必死不能活了。”
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 希西家就转脸朝墙,祷告耶和华说:
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 “耶和华啊,求你记念我在你面前怎样存完全的心,按诚实行事,又做你眼中所看为善的。”希西家就痛哭了。
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 耶和华的话临到以赛亚说:
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 “你去告诉希西家说,耶和华—你祖大卫的 神如此说:我听见了你的祷告,看见了你的眼泪。我必加增你十五年的寿数;
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 并且我要救你和这城脱离亚述王的手,也要保护这城。
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 “我—耶和华必成就我所说的。我先给你一个兆头,
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 就是叫亚哈斯的日晷,向前进的日影往后退十度。”于是,前进的日影果然在日晷上往后退了十度。
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 犹大王希西家患病已经痊愈,就作诗说:
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 我说:正在我中年之日 必进入阴间的门; 我余剩的年岁不得享受。 (Sheol h7585)
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol h7585)
11 我说:我必不得见耶和华, 就是在活人之地不见耶和华; 我与世上的居民不再见面。
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 我的住处被迁去离开我, 好像牧人的帐棚一样; 我将性命卷起, 像织布的卷布一样。 耶和华必将我从机头剪断, 从早到晚,他要使我完结。
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 我使自己安静直到天亮; 他像狮子折断我一切的骨头, 从早到晚,他要使我完结。
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 我像燕子呢喃, 像白鹤鸣叫, 又像鸽子哀鸣; 我因仰观,眼睛困倦。 耶和华啊,我受欺压, 求你为我作保。
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 我可说什么呢? 他应许我的,也给我成就了。 我因心里的苦楚, 在一生的年日必悄悄而行。
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 主啊,人得存活乃在乎此。 我灵存活也全在此。 所以求你使我痊愈,仍然存活。
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 看哪,我受大苦,本为使我得平安; 你因爱我的灵魂便救我脱离败坏的坑, 因为你将我一切的罪扔在你的背后。
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 原来,阴间不能称谢你, 死亡不能颂扬你; 下坑的人不能盼望你的诚实。 (Sheol h7585)
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol h7585)
19 只有活人,活人必称谢你, 像我今日称谢你一样。 为父的,必使儿女知道你的诚实。
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 耶和华肯救我, 所以,我们要一生一世 在耶和华殿中 用丝弦的乐器唱我的诗歌。
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 以赛亚说:“当取一块无花果饼来,贴在疮上,王必痊愈。”
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 希西家问说:“我能上耶和华的殿,有什么兆头呢?”
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

< 以赛亚书 38 >