< Job 8 >

1 Shuhi tami Bildad ni a pathung teh,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Nâsittouh maw he e hnonaw heh dei han, na pahni dawk hoi ka tâcawt e lawk hah athakaawme kahlî patetlah ao han.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Cathut ni kalan hoeh lah lawk a ceng boimaw, nahoeh pawiteh, Athakasaipounge ni, lannae a kamlang takhai boimaw.
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Na capanaw ni ama taranlahoi yon awh pawiteh, kâtapoenae kecu dawk a tâkhawng han.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Cathut hah atangcalah hoi, na tawng teh, Athakasaipounge koevah, kâheinae na sak pawiteh,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Tamikathoung tamikalan lah na awm pawiteh, nang hanelah atu roeroe thaw vaiteh, lanae hmuen koe hawinae na coe sak han.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Na kamtawngnae a thoung nakunghai, na poutnae a len katang han.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Bangkongtetpawiteh, pahrennae hoi a yan e hnonaw hah pakhingpalang haw, na mintoenaw ni a hmu e hnonaw hah pouk haw.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Bangkongtetpawiteh, paduem e tami la o awh teh, banghai panuek awh hoeh. Bangdawk tetpawiteh, talai van e hnin tha naw teh, tâhlip patetlah doeh ao.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Ahnimae lungthin thung hoi ka tâcawt e lawknaw ni, na dei pouh awh teh, na cangkhai hoeh namaw.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Tuinawk laipalah lungpum a roung thai han namaw. Tui laipalah capi teh a roung thai han namaw.
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 A hring nah tâtueng hoeh nakunghai, alouke akungnaw hlak palang a kamyai.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Cathut kapahnimnaw e a lamthung teh, hot patetlah ao. Tami kahawihoehnaw e ngaihawinae teh a kahma han.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 A kâuepkhai awh e teh, tâkhawng pouh lah ao han, a kâuepkhainae teh, Bombarui patetlah doeh ao.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 A im dawk a kamngawi ei kangdout thai hoeh. Kacakcalah a kuet ei pou cak thai ma hoeh.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Khobetnae koe dikkahringcala a roung teh, a kangnaw ni takha koung tahloi awh.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 A tangpha ni talung khakdeng teh, talung um vah a tangpha a payang nahane a tawng.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Amae hmuen koehoi phawk lah ao torei teh, pou kacak mahoeh, telah a kâpahnawt han.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Khenhaw! het hateh, lunghawinae lamthung lah a o, talai dawk hoi aloukenaw hah a pâw han.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Khenhaw! Cathut ni toun han kaawm hoeh e na tâkhawng hoeh vaiteh, thoe ka sak e teh kangdout sak mahoeh.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Na kâko teh panuinae hoi akawi sak vaiteh, na pahni hai lunghawinae lawk hoi akawi sak han.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Nang kahmuhmanaw hah yeiraipo sak vaiteh, tamikathoutnaw e rim teh awm mahoeh toe telah a ti.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >