< Luke 17 >

1 Jesus in a nungzui te tung ah, Mawna sung ah puk le khial thak ngawl tu sia suak thei ngawl hi: ahihang tabang a thengsak sia a mailam bing hi!
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 Patang no khat khialsak tu sang in, a ngawng ah an ngoaina suang khit in, tuipi sung ah ki khiasuk le, ama atu in phazaw hi.
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 Noma le noma kidawm vun: na suapui pa sia na tung ah hong khial le, tei in; a ki sikkik a hile, maisak in.
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 Na tung ah ni khat sung sali vei dong hong khial a, na tung ah sali vei dong hongpai in, kisik khi hi, hong cile, maisak in, ci hi.
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 Sawltakte in, Topa tung ah, ka upna uh hong khangsak tan, ci uh hi.
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 Taciang Topa in, Note in ankamci cia upna nei le uh te, hi theikung mun ah, na bul pan kilong in, tuipi sung ah ki phut in; ci le uh te, na thu hong ni tu hi.
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 Ahihang note sung ah khatpo in, lo tho, a hibale tuucing naseam khat nei in, tua naseampa lo pan hong cia pociang, pai in a, anne tu in to in, ci a kua in ci tu nu ziam?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 Ka an neak tu hong vawtkholsak tan a, an hong thuk tan, ka neak ka dawn man dong hong ngak tan, tua zawkciang in ne in a, dawn kik in; ci tu hi ngawl ziam01?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 Naseam pa in thupiak teng a vawt siat zawkciang a topa in lungdam a ko tu ziam? Ko tu um ngawl khi hi.
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 Tabangma in, note zong thupiak theampo na vawt siat zawk uh ciang, kote sia phattuam na nei ngawl naseam te ka hi uh hi, ka sep tu nasep a seam bekma khu hi, ci tavun, ci hi.
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 Jesus Jerusalem a pai ciang in Samaria le Galilee ngamngi tawn in pai hi.
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 Khua khat sung ah a tum uh ciang in, miphak sawm te taw kisi a, a khuala na ah ding in:
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 Jesus, Topa awng, hong hesuak tan, ci in a nging tatak in au uh hi.
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 Jesus in amate a mu ciang in, Pai tavun a, thiampi te kung ah noma le noma ki lak tavun, ci hi. Amate a pai uh laitak in, a vekpi in thiangtho siat uh hi.
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 Amate sung pan khat in damzo khi hi, ci a mu ciang in, heakkik a, aw ngingtak taw Pathian pok hi,
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 Taciang Jesus peang ah bok a, lungdam ko hi: ama sia Samaria mi a hihi.
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 Jesus in, Mihing sawm ki thiangsak hi ngawl ziam? Ahihang a dang kua te, koisung ah om ziam?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 Hi ngamdang mi simngawl Pathian pok tu in a heakkik mu ngawl khi hi, ci hi.
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 Taciang in Jesus in, Tho in a, pai in: na upna in hong damsak zo hi, ci hi.
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 Pharisee te in, Pathian kumpingam sia banghun ciang hong theng tu ziam? ci in Jesus dong uh hi, Jesus in, Pathian kumpingam sia mit taw mu thei in hong theng ngawl tu hi:
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 Hi mun ah en vun! a hibale, zesung ah en vun! ci in kuama in hong ci ngawl tu hi, banghangziam cile, en vun, Pathian kumpingam sia note sung ah om hi, ci hi.
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 Jesus in a nungzui te tung ah, Mihing Tapa ni sia, nikhat sung bek zong na mu nop mama uh hun hong theng tu hi, ahihang mu tha ngawl tu nu hi.
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 Note tung ah, hi mun ah en vun; a hibale, zesung ah en vun, hong ci tu uh hi: tabang te nung pan zui tha heak vun.
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 Banghangziam cile, khualeng sia, van mong khat pan mong khat dong a tang bang in, mihing Tapa ni zong tabangma hi tu hi.
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 Ahizong a masabel in ama in nasiatak thuak tu a, tu hun mihing te in nial tu uh hi.
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 Noah hunlai bangma in mihing Tapa hun ciang zong tabangma hi tu hi.
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 Noah tembaw sung tum a, tuiliim in mi theampo a bocip siat dong, amate ne le dawn, mopui motha in om tek uh hi.
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 Tasia bangma in Lot hun lai zong amate ne le dawn, van zuak, thingkung cing le inn sa in om tek uh hi;
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 Ahihang Lot sia Sodom khua pan a pusua ni ciang in, van pan mei le kat sia ngua bang in zu a, a vekpi in susia siat hi.
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 Mihing Tapa hong ki pualak ni ciang zong tabangma hi tu hi.
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 Tua ni ciang in, innkhum tung a om te, innsung ah van la tu in tuaksuk nawn heak hen: lo ah a omte zong inn ah ciakik nawn heak hen.
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 Lot i zi na phawk tavun.
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 A kuamapo ama nuntakna a hung nuam peuma a nuntakna sum tu hi; a kuamapo a ma nuntakna a sum peuma nuntakna nga tu hi.
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 Keima in kong ci hi, tua ni zan ciang lupna khat tung ah mi ni lumkhawm tu hi; khat ki la tu a, khat ki nusia tu hi.
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 Numei ni an ngoai khawm tu hi; khat ki la tu a, khat ki nusia tu hi.
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 Pasal ni lo sung ah na seam khawm tu hi; khat kila tu a, khat ki nusia tu hi, ci hi.
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 Ama te in, Topa, koisung hi tu ziam? ci in dong uh hi, Jesus in amate tung ah, Mithi luang om na mun theampo ah vaciik te ki kaikhawm tu hi, ci in zo kik hi.
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< Luke 17 >