< Olcueih 28 >

1 Halang tah a hloem pawt akhaw rhaelrham khing. Tedae aka dueng tah sathueng bangla amah pangtung uh.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Khohmuen kah boekoek dongah mangpa la yet dae, aka yakming hlang long tah a ming dongah a ram a pai sak.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 Hlang he khodaeng loh tattloel patoeng a hnaemtaek he khaw, khotlan loh bet a kawt tih buh a om pawt bangla om.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Olkhueng aka hnoo rhoek loh halang te a thangthen uh. Tedae olkhueng aka tuem long tah amih te a huek.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Hlang thae rhoek loh tiktamnah te yakming uh pawt dae, BOEIPA aka tlap rhoek loh boeih a yakming uh.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 A thincaknah neh aka pongpa khodaeng he, longpuei kawnvoi dongkah hlanglen lakah then.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Olkhueng aka kueinah capa long tah a yakming dae, carhut neh aka luem loh a napa kah hmai a thae sak.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 A casai a puehkan neh a boeirhaeng aka tom long khaw, tattloel aka rhen ham ni a puehkan la a coi pah coeng.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Olkhueng a yaak lalah a hna tlap tlap aka khong tah, a thangthuinah khaw tueilaehkoi la om.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Aka thuem te longpuei thae la aka palang sak tah cakhom ah amah lah cungku ni. Tedae cuemthuek rhoek long tah hnothen a pang uh ni.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 Hlanglen pa he a mikhmuh ah amah aka cueih koek la ngai uh dae, tattloel long khaw aka yakming long tah anih te a khe.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Aka dueng rhoek a sundaep vaengah muep boeimang tangloeng dae, halang rhoek a thoh vaengah tah hlang loh a thuh tak.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 A boekoek aka phah he a thaihtak moenih. Tedae aka phoe tih aka hnoo tah a haidam.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Aka rhih yoeyah hlang tah a yoethen dae, a lungbuei aka mangkhak loh boethae khuila cungku.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Halang loh a taemrhai vaengah pilnam tattloel te sathueng bangla a nguel thil tih vom bangla cu.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 A lungcuei aka talh rhaengsang tah tlungalnah yet. Mueluemnah aka hmuhuet la aka hmuhuet tah a hinglung vang ni.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Hinglu kah thii neh hlang aka hnaemtaek hlang tah vaam khuila rhaelrham cakhaw, anih te duel mahpawh.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Cuemthuek la aka pongpa tah daem tih, longpuei aka kawn sak tah vaikhat lam ni a cungku eh.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Amah khohmuen aka tawn tah caak khaw kum ni. Tedae a hoenghoep bueng aka hloem tah khodaeng la hah ni.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Uepomnah hlang kah yoethennah tah yet. Tedae boei hamla aka tanolh khaw hmil mahpawh.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 Maelhmai a loha khaw then pawh. Tedae buh kamat dongah ni hlang loh boe a koek.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Hlang moeithae loh boeirhaeng dongah ngawn tah hlawt let dae, vaitahnah loh anih a thoeng thil te ming pawh.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Hlang aka tluung he a hnukah tah a lai aka hnal lakah, mikdaithen la om.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 A manu neh a napa a rheth lalah boekoek pawt la aka thui tah, kut aka yook ham hlang kah a pueipo la om.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Mungkung kah hinglu long tah olpungkacan a huek. Tedae BOEIPA dongah aka pangtung ni a hoeikhang eh.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Amah kah lungbuei dongah aka pangtung tah amah te ang coeng. Tedae cueihnah dongah aka pongpa tah amah khaw hlawt uh.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Khodaeng taengah aka pae tah a tloelnah om pawh. Tedae a mik aka him tah tapvoepnah muep kum.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Halang rhoek a thoh vaengah hlang loh a thuh tak. Tedae a milh vaengah aka dueng rhoek khaw pul.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Olcueih 28 >