< Olcueih 20 >

1 Misurtui tah hmuiyoi la om tih yu long khaw hue a sak. Te dongah anih loh a palang sak hlang boeih tah cueih voel pawh.
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 Manghai kah a mueirhih tah sathueng kah a kawk bangla om tih, anih aka paan ngawn tah a hinglu ni a phai coeng.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 Tuituknah lamloh aka hoep uh hlang ham thangpomnah la om tih, aka ang boeih long tah tohhaemnah a puek sak.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 Kolhnaw loh sikca ah pataeng caai voel pawh. Te dongah cangah ah a dawt tah a dawt dae dang voel pawh.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 Hlang lungbuei kah cilsuep tah tui aka dung bangla om tih, hlang lungcuei loh a dueh.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Hlang pilnu amah kah sitlohnah te boeih a doek dae, oltak hlang te u long a hmuh?
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 A thincaknah neh aka cet hlang dueng tah amah hnukah a ca rhoek khaw a yoethen.
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Manghai tah laitloeknah ngolkhoel dongah ngol tih, boethae boeih te a mik neh a thaek.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 “Ka lungbuei ka saelh tih ka tholh lamloh ka caihcil,” tila ulong a ti thai.
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 Lungto neh lungto khaw, cangnoek neh cangnoek khaw BOEIPA ham a boktlap la tueilaehkoi ni.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 A khoboe dongah camoe pataeng khaw loha coeng. A bisai loh cil tih a thuem atah.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 Hna loh yaak tih mik loh a hmuh he khaw a boktlap la BOEIPA long ni a saii.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Ih he lungnah boeh na khodaeng na pang ve. Na mik a tueng daengah ni buh na cung eh.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 Hno aka lai loh a thae, a thae la a thui tih amah a khawk vaengah tah lat thangthen bal.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Sui neh lungvang he khawk mai dae, mingnah hmuilai he tah umponah hnopai bangla kuel.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Kholong ham rhi a khang pah vaengkah a himbai neh kholong nu, kholong nu ham a laikoi pah te khaw lo laeh.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Laithae buh he hlang hamla tui dae, a hnukah a ka dongah lungcang muep baetawt.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Kopoek he cilsuep neh cikngae sak lamtah, caemtloek khaw a niing khueh lah.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Baecenol he caemtuh loh a hliphen tih a caeh puei. Te dongah a ka neh aka hloih te rhikhang pah boeh.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 A manu neh a napa aka hnaep tah a hmaithoi a thih pah vetih, yinthuem kah yinthuem ah hmaisuep la om ni.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 Rho he khaw a lamhma lah banlak a kawt dae, a hmailong ah a yoethen mahpawh.
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 A thae te, “Ka thuung van ni,” ti nah boeh. BOEIPA mah lamtawn lamtah namah te ng'khang bitni.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Coilung neh coilung khaw BOEIPA kah a tueilaehkoi ni. Te dongah hlangthai palat kah cooi tah a then moenih.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 Hlang kah a khokan he BOEIPA taeng lamkah ni. Te dongah hlang loh a longpuei te metlam a yakming eh?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 Hmuencim te a cukhat thil tih olcaeng hnukah a hnukdawn te hlang ham hlaeh la om.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Manghai aka cueih loh halang rhoek te a thaek tih, amih te lengkho neh a paluet thil.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 BOEIPA kah hmaithoi long tah hlang kah a hiil neh a bungko kah a khui khaw boeih a thaih.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 Sitlohnah neh oltak loh manghai te a kueinah tih, sitlohnah loh a ngolkhoel a duel pah.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 Tongpang rhoek kah a thadueng tah amamih kah a boei a mang la om tih, sampok he khaw patong rhoek kah rhuepomnah ni.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Tloh kah a hma a met vanbangla, bungko khui kah hmasoe loh a thae a cing sak.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

< Olcueih 20 >