< Olrhaepnah 18 >

1 Israel taengkah khoyo neh rho he Levi koca boeih lamkah Levi khosoih ham a om oeh pawt dongah BOEIPA kah hmaihlutnah te amah rho la ca uh van saeh.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 Te dongah a manuca lakli ah pataeng anih ham rho om pawt vetih anih taengkah a thui pah vanbangla BOEIPA amah ni anih kah rho la aka om coeng.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 Pilnam loh hmueih la a ngawn te khosoih rhoek kah hamsum la om vetih vaito khaw, tu khaw a laeng, a kam neh a kotak te khosoih pae saeh.
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 Na cangpai vueilue, misur thai a huem, na situi, tu mul tanglue te khaw na paek ni.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 A hing tue khui boeih ah BOEIPA amah ming neh bibi la aka pai ham ni nang koca rhoek boeih khui lamloh anih koca rhoek tah BOEIPA na Pathen loh amah hut la a coelh.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 Levi pakhat loh na vongka khui lamloh puen uh coeng. Tedae BOEIPA hmuen tuek te a hinglu loh a hue tangkik vaengah a bakuep nah Israel kho khat khat la koep ha pawk atah,
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 BOEIPA mikhmuh ah aka pai a manuca Levi rhoek vanbangla BOEIPA na Pathen ming neh bibi saeh.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 A napa taengkah hnoyoih om mai cakhaw khoyo tah khoyo bangla ca uh saeh.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 BOEIPA na Pathen loh nang taengah m'paek khohmuen te na kun thil vaengah amih namtom rhoek kah tueilaehkoi te saii hamla cang boeh.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Hmai dongah a capa a canu aka thak, bihma aka bi, kutyaek aka so, lung aka so, hlang aka bi,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 Hlang hloih neh aka yok uh khaw, rhaitonghma aka dawt khaw, hnam neh hlang duek aka khue khaw na khuiah nuen boel saeh.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 Te bang aka saii boeih te BOEIPA kah a tueilaehkoi tih te rhoek kah tueilaehkoi dong ah ni amih khaw BOEIPA na Pathen loh na mikhmuh lamkah a haek.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 BOEIPA na Pathen taengah a cuemthuek la na om ni.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 Nang kah na huul namtom rhoek loh kutyaek aka so tih aka hma ol te hnatun uh cakhaw nang ham tah BOEIPA na Pathen loh a ngaih moenih.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 BOEIPA na Pathen loh namah khui lamkah na manuca tonghma, kai bang he nangmih ham a thoh bitni. Anih ol te hnatun uh.
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 Horeb kah hlangping hnin vaengah BOEIPA na Pathen taengah boeih na dawt tih, “BOEIPA ka Pathen ol yaak hamla ng'khoep boel mai lamtah hmai puei he khaw m'hmuh sak voel boel mai. Te daengah ni ka duek pawt eh?,” na ti nah vanbangla,
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 BOEIPA loh kai taengah, “A thui uh te thuem.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 Amih khuikah a manuca tonghma nang bang te ka thoh vetih a ka dongah ka ol ka khueh pah vaengah anih ka uen boeih te amih taengah a thui bitni.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 Kai ming neh a thui kai kah olka te hnatun mueh la aka om hlang te tah kamah loh ka cae bitni.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 Tedae lokhak tih thui ham koi te anih ka uen pawt mai ah ka ming neh olka aka thui tonghma te khaw, a tloe pathen ming neh aka cal tonghma te duek saeh,” a ti.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 Tahae ah khaw na thin khuiah ngawn tah, “BOEIPA loh anih voek pawt koinih olka te metlamlae m'ming uh thai,” na ti mai ni.
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 Tonghma pakhat long he BOEIPA ming neh a thui dae hno pakhat khaw coeng sak pawt tih a olka te a thaihtak pawt atah BOEIPA kah a thui moenih. Althanah neh aka cal tonghma tah a taengah bakuep pah boeh.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Olrhaepnah 18 >