< 2 Manghai 8 >

1 Elisha loh a capa aka hing huta te a voek tih, “Thoo lamtah namah neh na imkhui te cet uh laeh. Na bakuep nah noek ah bakuep mai. BOEIPA loh khokha ham a khue dongah khohmuen ah he kum rhih khuiah pai pueng ni,” a ti nah.
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 Te dongah huta te thoo tih Pathen hlang kah ol bangla a saii. Amah neh a imkhui te a caeh puei tih Philisti khohmuen ah kum rhih bakuep.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 Kum rhih kah a bawtnah a pha vaengah tah huta te Philisti khohmuen lamloh mael. Te vaengah cet tih amah imkhui ham neh a khohmuen ham te manghai taengah pang.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 Manghai loh Pathen hlang kah tueihyoeih Gehazi te a voek tih, “Elisha loh hno len cungkuem a saii te kai taengah tae laeh,” a ti nah.
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 Te dongah aka duek tangtae a hing sak tih a capa koep aka hing huta loh a imkhui ham neh a khohmuen ham manghai taengah a pang te khaw manghai taengah a tae pah. Te phoeiah Gehazi loh, “Ka boei manghai aw, he huta he ni a capa Elisha loh a hing sak pah.
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 Manghai loh huta te a dawt tih a taengah a tae pah vaengah tah manghai loh anih ham te imkhoem pakhat a khueh pah tih, “Khohmuen a hnoong khohnin lamloh tahae hil khohmuen kah a vueithaih cungkuem te anih taengah boeih mael laeh,” a ti nah.
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 Elisha te Damasku la a caeh vaengah Aram manghai Benhadad te ana tlo. Te dongah a taengla a puen pah tih, “Pathen kah hlang he la ha pawk,” a ti nah.
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 Manghai loh Hazael te, “Na kut dongah khocang khuen lamtah Pathen kah hlang doe hamla cet laeh. Anih lamloh BOEIPA te dawt lah, he tloh lamloh ka hing venim?' dawt lah,” a ti nah.
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 Te dongah anih doe hamla Hazael te cet tih a kut dongah khocang neh Damasku kah thennah cungkuem te kalauk sawmli phueih la a khuen. Cet tih a mikhmuh ah a pai vaengah tah, “Na capa Aram manghai Benhadad loh kai he nang taengla n'tueih, 'He tloh lamloh ka hing aya?' a ti,” a ti nah.
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 Elisha loh anih te, “Cet lamtah amah taengah, 'Na hing rhoe na hing ni, 'ti nah. Tedae BOEIPA loh kai n'tueng coeng dongah duek rhoe duek ni,” a ti nah.
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Te phoeiah tah a maelhmai te a khueh, a khueh tih a yah hil Pathen kah hlang te a rhah pah.
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 Te vaengah Hazael loh, “Ka boeipa balae tih na rhah,” a ti nah hatah, “Israel ca rhoek taengah boethae na saii ham khaw, amih kah hmuencak te hmai neh na hlae ham khaw, amih kah tongpang rhoek te cunghang neh na ngawn ham khaw, amih kah camoe rhoek te na til ham khaw, aka vawn te na boe ham khaw ka ming dongah,” a ti nah.
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Tedae Hazael loh, “Na sal ui loh metlam hno len a saii eh?” a ti nah. Elisha loh, “Aram soah na manghai ham te BOEIPA loh kai n'tueng coeng,” a ti nah.
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 Elisha taeng lamloh nong tih a boei taengla a pawk vaengah anih te, “Elisha loh nang taengah balae a thui,” a ti nah. Te vaengah, “Kai taengah tah, ' Na hing rhoe na hing ni, ' a ti,” a ti nah.
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 Tedae a vuen pha vaengah himbai thah a loh tih tui khuila a nuem phoeiah manghai kah maelhmai te a dah pah. Te vaengah manghai te duek tih Hazael te anih yueng la manghai.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 Israel manghai Ahab capa Joram kah a kum nga dongkah, Judah manghai Jehoshaphat phoeiah tah, Judah manghai Jehoshaphat capa Jehoram te manghai.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 Kum sawmthum kum nit a lo ca vaengah anih te manghai tih Jerusalem ah kum, kum rhet manghai.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 Anih khaw Israel manghai rhoek kah longpuei ah pongpa. Ahab canu te anih yuu la a om dongah Ahab imkhui kah a saii bangla BOEIPA mikhmuh ah boethae a saii.
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 A sal David amah taengah a thui bangla anih ham neh a ca rhoek ham hnin takuem hmaithoi a khueh pah ham dongah ni BOEIPA loh Judah te phae a ngaih pawh.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 Anih tue vaengah ni Edom loh Judah kut hmui lamkah boe a koek tih amamih ham manghai a manghai sak.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 Joram te amah taengkah leng boeih neh Zair te a paan. Khoyin ah thoo tih Edom te a tloek. A kaepvai te amah neh leng mangpa rhoek loh a dum vaengah pilnam tah amah dap la rhaelrham coeng.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 Edom tah tahae khohnin duela Judah kut hmui lamloh boe a koek. Libnah khaw te vaeng tue ah boe a koek coeng.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 Joram kah ol noi neh a saii boeih te khaw Judah manghai rhoek kah khokhuen olka cabu dongah a daek uh moenih a?
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 Joram te a napa rhoek taengla a khoem uh vaengah David khopuei ah a napa rhoek taengah a up. Te phoeiah a capa Ahaziah te anih yueng la manghai.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Israel manghai Ahab capa Joram kah kum hlai nit kum vaengah Judah manghai Jehoram capa Ahaziah te manghai van.
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 Ahaziah he kum kul kum nit a lo ca vaengah manghai tih Jerusalem ah kum khat manghai. A manu ming tah Israel manghai Omri canu Athaliah ni.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 Anih he Ahab imkhui loh a cava nah dongah Ahab imkhui kah longpuei ah pongpa tih BOEIPA mikhmuh ah Ahab imkhui bangla boethae a saii.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Ahab capa Joram neh Ramothgilead kah Aram manghai Hazael te caem la a paan vaengah Arammi loh Joram te a ngawn.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 Te dongah manghai Joram khaw Aram manghai Hazael a vathoh thil vaengkah Ramah ah Arammi loh a ngawn. Te hmasoe te hoeih sak ham Jezreel la mael. Tedae anih te a nue coeng dongah Judah manghai Jehoram capa Ahaziah khaw Ahab capa Joram te sawt hamla Jezreel la suntla.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< 2 Manghai 8 >