< Joba 8 >

1 Shuhi Bildad loh a doo tih,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “He he me hil nim na thui ve? Na ka kah ol tah khohli bangla khuet coeng.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Pathen loh tiktamnah he a khun sak tih, Tlungthang loh duengnah te a khun sak mai a?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Na ca rhoek te anih taengah a tholh vaengah, amih te amamih kah boekoek kut dongla a tueih.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Namah loh Pathen te na toem tih Tlungthang te na hloep mak atah,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Na cil tih na thuem koinih nang yueng la haenghang vetih na duengnah rhamtlim te n'thuung pataeng pawn ni.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Na tongnah te a yiit la om cakhaw na hmailong te muep rhoeng ni.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Lamhma kah cadil taengah dawt laeh lamtah, a napa rhoek khenah te soepsoei laeh.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Mamih loh n'hlaem kah khaw m'ming uh moenih, mamih kah khohnin tah diklai mueihlip dongkah ni.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Amih te na thuinuet pawt tih a, nang taengah a thui vetih, amih kah lungbuei lamloh olthui te a khueh eh?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Nongtui pawt ah talik thawn tih, tui om mueh ah capu rhoeng a?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Te te a duei pueng ah a hlaek pawt akhaw, sulrham boeih hmai ah rhae coeng.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Pathen aka hnilh boeih kah caehlong neh lailak kah ngaiuepnah tah bing tangloeng.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 A uepnah neh a pangtungnah bumba im te khaw bawtboeng.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 A im dongah hangdang dae pai thai pawh. Te te a kuel dae thoo pawh.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Anih te khosae li ah thingsup tih a dum ah a dawn sai.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 A yung loh lungkuk dongah a ven tih lungto im te a hmuh.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Te te a hmuen lamloh a phuk van vaengah, ‘Nang kam hmu moenih,’ anih te a namnah.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 He he a longpuei kah omthennah coeng koinih laipi tloe lamloh a poe uh khaming.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Pathen loh cuemthuek hnawt ngawn pawt tih thaehuet kut te a moem moenih.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Na ka dongah nueihbu neh na hmui dongah tamlung bae.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Na lunguet rhoek loh yahpohnah a bai uh vetih halang kah dap tah om mahpawh,” a ti.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Joba 8 >