< Genesis 7 >

1 Angraeng mah Noah khaeah, Nangmah hoi na imthung takoh boih palong thungah akun oh; nang loe ka hmaa ah vaihi dung ih kaminawk salakah kami katoeng ah kang hnuk.
Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
2 Long nuiah taw ih moi atii anghmat ving han ai ah, atii kamghnong kaciim moi to amno hoi ampa sarihto, acaeng kanghmong kaciim ai moi doeh amno hoi ampa hnetto,
Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
3 atii kanghmong van ih tavaa doeh amno hoi ampa sarihto ah la boih ah.
Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
4 Vaihi hoi ni sarihto thungah, long ah ni qui palito hoi qum qui palito thung kho kang oihsak moe, long nuiah kaom ka sak ih kahing hmuennawk to kam rosak boih han, tiah a naa.
Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
5 Angraeng mah thuih ih lok baktih toengah Noah mah sak boih.
Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
6 Long to tui mah uem naah, Noah loe saning cumvai tarukto oh boeh.
Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
7 Tui len pongah, Noah mah a capanawk, a zu hoi a capanawk ih zu boih, palong thungah akun haih.
Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
8 Kaciim hoi kaciim ai moinawk, tavaanawk hoi long ah kavak moinawk boih,
Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
9 Sithaw mah Noah khaeah thuih ih lok baktih toengah, amno hoi ampa hnetto kacung ah, Noah hoi nawnto palong thungah akun o.
Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
10 Ni sarihto pacoengah loe long nuiah tui uemhaih to phak.
Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
11 Noah hinghaih saning cumvai tarukto koephaih saning, khrah hnetto haih, ni hatlai sarihto naah, kalen hoi kathuk long thung hoiah tui to puek moe, van thokbuemnawk to am-ongh.
Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
12 Ni qui palito hoi qum qui palito long nuiah kho angzoh.
Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
13 To na niah Noah loe a capa Shem, Ham hoi Japheth, a zu hoi a capa thumto ih zunawk,
Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
14 Moi kasannawk, pacah ih moinawk boih, long ah kavak moi, pakhraeh tawn tavaanawk loe Noah hoi nawnto palong thungah akun o.
Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
15 Hinghaih tawn, moinawk boih loe hnetto kacung ah, Noah khaeah caeh o moe, palong thungah akun o.
Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
16 Sithaw mah Noah khaeah thuih ih lok baktih toengah, moinawk boih amno hoi ampa kacung ah, Noah khaeah palong thungah akun o; to pacoengah Angraeng mah anih to thok khah thuih khoep.
Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
17 Long loe ni qui palito thung tui mah uem; kalen aep aep tui mah palong to long ranui ah atoengh tahang.
Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
18 Tui loe len moe, long ranui bangah sang tahang aep aep; tui mah palong to long ranui ah atoengh tahang.
Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
19 Long nuiah tui len parai pongah, van tlim ah kaom, maesangnawk to tui mah uem boih.
Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
20 Mae ranuih dong hatlai panga karoek to tui mah uengh tahang.
Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
21 Long ah kaom angtawt thaih moinawk, tavaanawk, pacah ih moinawk, taw ih moisannawk, long ah kavak moinawk hoi kaminawk to duek o boih.
Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
22 Saoeng ah kaom, hnah hoi anghahaih takhi tawn moinawk to duek o boih.
Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
23 Long nuiah kaom kahing hmuennawk, kami, pacah ih moi, long ah kavak moinawk, van ih tavaanawk to tamit boih; Noah angmah, anih hoi nawnto kaom kaminawk khue ni anghmat o.
Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
24 Tui mah long to ni cumvai, qui pangato thung uem.
Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood