< Zefaniya 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Teško gradu odmetnièkom i oskvrnjenom, nasilnièkom!
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Ne sluša glasa, ne prima nauka, ne uzda se u Gospoda, ne pristupa k Bogu svojemu.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Knezovi su mu u njemu lavovi koji rièu; sudije su mu vuci veèernji, koji ne gloðu kosti do jutra.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Proroci su mu hvališe, varalice; sveštenici njegovi skvrne svetinju, izvræu zakon.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Gospod je pravedan usred njega, ne èini nepravde, svako jutro iznosi sud svoj na vidjelo, ne izostaje, ali bezbožnik ne zna za stid.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
Istrijebih narode, kule im se razoriše, ulice im opustih, te niko ne prolazi; gradovi im se raskopaše, da nema nikoga, nema stanovnika.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Rekoh: pobojaæeš me se, primiæeš nauk; neæe mu se zatrti stan nièim su èim bih ga pohodio; ali oni uraniše te pokvariše sva djela svoja.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Zato èekajte me, govori Gospod, do dana kad æu se podignuti na plijen; jer je sud moj da saberem narode i pokupim carstva, da izlijem na njih gnjev svoj, svu žestinu jarosti svoje, jer æe oganj revnosti moje proždrijeti svu zemlju.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Jer æu tada promijeniti narodima usne, te æe biti èiste, da bi svi prizivali ime Gospodnje i služili mu složnijem ramenima.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Ispreko rijeka Huskih koji se meni mole, rasijani moji, donijeæe mi dare.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
Tada se neæeš više stidjeti nijednoga svojih djela, kojima si mi zgriješio; jer æu onda uzeti iz tebe one koji se hvale slavom tvojom, i neæeš se više velièati na svetoj gori mojoj.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
I ostaviæu u tebi narod nevoljan i siromašan, i oni æe se uzdati u ime Gospodnje.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Ostatak Izrailjev neæe èiniti bezakonja niti æe govoriti laži, niti æe se naæi u ustima njihovijem jezik prijevaran; nego æe pasti i ležati i neæe biti nikoga da ih plaši.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Pjevaj, kæeri Sionska; klikuj, Izrailju; raduj se i veseli se iz svega srca, kæeri Jerusalimska!
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Ukloni Gospod sudove tvoje, odvrati neprijatelje tvoje; car Izrailjev Gospod usred tebe je, neæeš se više bojati zla.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
U onaj dan reæi æe se gradu Jerusalimu: ne boj se; Sionu: nemoj da ti klonu ruke.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Gospod Bog tvoj, koji je usred tebe, silni, spašæe te; radovaæe ti se veoma, umiriæe se u ljubavi svojoj, veseliæe se tebe radi pjevajuæi.
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Koji tuže za praznicima, sabraæu ih, koji su iz tebe, radi teške sramote koja je na tebi.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Gle, uništiæu u ono vrijeme sve koji te muèe, i izbaviæu hrome i sabrati odagnane, i dobaviæu im hvalu i slavu po svoj zemlji, gdje su bili pod sramotom.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
U ono vrijeme dovešæu vas, u ono vrijeme sabraæu vas; jer æu vam dobaviti slavu i hvalu po svijem narodima na zemlji, kad povratim roblje vaše pred vašim oèima, govori Gospod.

< Zefaniya 3 >