< Zefaniya 2 >

1 Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi, inu mtundu wochititsa manyazi,
Saberite se, saberite se, narode nemili,
2 isanafike nthawi yachiweruzo, nthawi yanu isanawuluke ngati mungu, usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova, tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
Dok nije izašao sud, i dan prošao kao pljeva, dok nije došao na vas ljuti gnjev Gospodnji, dok nije došao na vas dan gnjeva Gospodnjega.
3 Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko, inu amene mumachita zimene amakulamulani. Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa; mwina mudzatetezedwa pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Tražite Gospoda svi koji ste krotki u zemlji, koji èinite što je naredio; tražite pravdu, tražite krotost, eda biste se sakrili na dan gnjeva Gospodnjega.
4 Gaza adzasiyidwa ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja. Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu ndipo Ekroni adzazulidwa.
Jer æe se Gaza ostaviti i Askalon æe opustjeti; Azot æe se odagnati u podne i Akaron æe se iskorijeniti.
5 Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu mtundu wa Akereti; mawu a Yehova akutsutsa iwe Kanaani, dziko la Afilisti. “Ndidzakuwononga ndipo palibe amene adzatsale.”
Teško onima koji žive po bregovima morskim, narodu Heretejskom: rijeè je Gospodnja na vas, Hanane, zemljo Filistejska, ja æu te zatrti da ne bude stanovnika u tebi.
6 Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti, lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
I bregovi æe morski biti stanovi i jame pastirske i torovi za stada.
7 Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda; adzapezako msipu. Nthawi ya madzulo adzagona mʼnyumba za Asikeloni. Yehova Mulungu wawo adzawasamalira; adzabwezeretsa mtendere wawo.
I taj æe kraj biti ostatku doma Judina; ondje æe pasti; u domovima æe Askalonskim lijegati uveèe; jer æe ih pohoditi Gospod Bog njihov i povratiti roblje njihovo.
8 “Ndamva kunyoza kwa Mowabu ndi chipongwe cha Amoni, amene ananyoza anthu anga ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
Èuo sam rug Moavov i ukore sinova Amonovijeh kojima ružiše moj narod, i raširiše se preko meða njihovijeh.
9 Choncho, pali Ine Wamoyo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, “Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu, Amoni adzasanduka ngati Gomora; malo a zomeramera ndi maenje a mchere, dziko la bwinja mpaka muyaya. Anthu anga otsala adzawafunkha; opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
Zato, tako ja bio živ, govori Gospod nad vojskama, Bog Izrailjev, Moav æe biti kao Sodom i sinovi Amonovi kao Gomor, mjesto koprivama, i slanica i vjeèna pustoš: ostatak naroda mojega oplijeniæe ih, i koji ostanu od naroda mojega naslijediæe ih.
10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo, chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
To æe im biti za ponositost njihovu; jer ružiše narod Gospoda nad vojskama i podizaše se na nj.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo. Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira, uliwonse ku dziko la kwawo.
Strašan æe im biti Gospod, jer æe istrijebiti sve bogove zemaljske, i njemu æe se klanjati svaki iz svojega mjesta, sva ostrva narodna.
12 “Inunso anthu a ku Kusi, mudzaphedwa ndi lupanga.”
I vi, Etiopljani, biæete pobijeni maèem mojim.
13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto ndi kuwononga Asiriya, kusiya Ninive atawonongekeratu ndi owuma ngati chipululu.
I dignuæe ruku svoju na sjever, i zatræe Asirsku, i Nineviju æe opustiti da bude suha kao pustinja.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko, pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse. Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu adzakhala pa nsanamira zake. Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera, mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha, nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
I u njoj æe ležati stada, svakojako zvijerje izmeðu naroda, i gem i æuk noæivaæe na dovratnicima njezinijem; glasom æe pjevati na prozorima; pustoš æe biti na pragovima, jer æe se poskidati kedrovina.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala umene kale unali wotetezedwa. Unkanena kuti mu mtima mwake, “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.” Taonani lero wasanduka bwinja, kokhala nyama zakutchire! Onse owudutsa akuwunyoza ndi kupukusa mitu yawo.
Taki æe biti veseli grad, koji sjedi bez brige, koji govori u srcu svom: ja sam, i osim mene nema drugoga. Kako opustje! posta loža zvijerju! Ko god proðe mimo nj zviždaæe i mahati rukom.

< Zefaniya 2 >