< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
The word of Yahweh which came unto Zephaniah, son of Cushi, son of Gedaliah, son of Amariah, son of Hezekiah, —in the days of Josiah son of Amon, king of Judah.
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
I will take clean away everything from off the face of the ground, Declareth Yahweh.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
I will take away man and beast, I will take away the bird of the heavens and the fishes of the sea, and the stumblingblocks, even them who are lawless, —and will cut off mankind, from off the face of the ground, Declareth Yahweh.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
And I will stretch out my hand—over Judah, and over all the inhabitants of Jerusalem, —and will cut off out of this place, the name of Baal, the name of the priestlings, with the priests;
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
And them who bow down upon the housetops to the host of the heavens, —and them who bow down—who swear to Yahweh, and swear by Milcom;
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
And them who turn away from following Yahweh, —and have neither sought Yahweh, nor enquired for him.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Hush! at the presence of My Lord, Yahweh, —for, near, is the day of Yahweh, for Yahweh hath prepared his sacrifice, hath hallowed his guests.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
And it shall come to pass, in the day of Yahweh’s sacrifice, that I will punish the rulers, and the sons of the king, —and all such as are clothed with foreign apparel;
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
And I will punish every one who leapeth over the threshold, in that day, —those who fill the house of their lords with violence and deceit.
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
And there shall come to be, in that day, declareth Yahweh, The noise of an outcry from the fish-gate, and of a howling out of the new city, —and of a great crashing, from the hills.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Howl, ye inhabitants of the lower city, —because destroyed are all the people of traffic, cut off are all they who were laden with silver.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
And it shall come to pass, at that time, that I will search through Jerusalem, with lamps, —and will punish the men who are thickened upon their lees, who are saying in their heart, Yahweh, will not give blessing, neither will he bring calamity.
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Therefore shall their goods become a booty, and their houses, a desolation, —and they shall build houses, but not inhabit them, and plant vineyards, but not drink the wine thereof.
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
Near is the great day of Yahweh, near, and very speedy, —The noise of the day of Yahweh, a strong man—there!—bitterly crying out!
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
A day of indignation, —that day! day of danger and distress, day of rush, and of crash, day of obscurity, and deep gloom, day of cloud, and thick darkness;
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
day of horn, and war-shout, —against the fortified cities, and against the high towers.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
And I will bring distress to mankind, and they shall walk like them who are blind, because, against Yahweh, have they sinned, —and their blood, shall be poured out, as dust, and their bowels like dung.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Neither their silver nor yet their gold, shall be able to deliver them, in the day of the indignation of Yahweh, but, in the fire of his jealousy, shall the whole earth be consumed; For, a destruction, surely a terrible one, will he make, with all them who dwell in the earth.

< Zefaniya 1 >