< Zekariya 7 >

1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
And it is maad in the fourthe yeer of Darius, kyng, the word of the Lord was maad to Sacarie, in the fourthe dai of the nynthe monethe, that is Caslew.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
And Sarasar, and Rogumelech, and men that weren with hem, senten to the hous of the Lord, for to preye the face of the Lord;
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
that thei schulden seie to prestis of the hous of the Lord of oostis, and to profetis, and speke, Whether it is to wepe to me in the fyuethe monethe, ether Y schal halowe me, as Y dide now many yeeris?
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord was maad to me,
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
and seide, Speke thou to al the puple of the lond, and to prestis, and seie thou, Whanne ye fastiden, and weiliden in the fyueth and seuenthe monethe, bi these seuenti yeeris, whether ye fastiden a fast to me?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
And whanne ye eeten, and drunken, whether ye eten not to you, and drunken not to you silf?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Whether wordis of profetis ben not, whiche the Lord spak in the hond of the formere profetis, whanne yit Jerusalem was enhabited, and was ful of richessis, and it, and citees therof in cumpas therof, and at the south and in feeldi place was enhabited?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
And the word of the Lord was maad to Sacarie, and seide, The Lord of oostis saith these thingis, and spekith,
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Deme ye trewe dom, and do ye merci, and doyngis of merci, ech man with his brother.
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
And nyle ye falsli calenge a widewe, and fadirles, ether modirles, and comelyng, and pore man; and a man thenke not in his herte yuel to his brother.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
And thei wolden not `take heede, and thei turneden awei the schuldre, and yeden awei, and `maden heuy her eeris, lest thei herden.
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
And thei puttiden her herte as adamaunt, lest thei herden the lawe, and wordis whiche the Lord of oostis sente in his Spirit, bi the hond of the formere profetis; and greet indignacioun was maad of the Lord of oostis.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And it is doon, as he spak; and as thei herden not, so thei schulen crie, and Y schal not here, seith the Lord of oostis.
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
And Y scateride hem bi alle rewmes, whiche thei knewen not, and the lond is desolat fro hem; for that there was not a man goynge and turnynge ayen, and thei han put desirable lond in to desert.

< Zekariya 7 >