< Zekariya 14 >

1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Oto przychodzi dzień PANA, a twój łup będzie rozdzielony pośród ciebie.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
Zgromadzę bowiem do bitwy wszystkie narody przeciwko Jerozolimie, a miasto zostanie zdobyte, domy splądrowane i kobiety zgwałcone. Połowa miasta pójdzie do niewoli, a resztka ludu nie będzie wygnana z miasta.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Wtedy PAN wyruszy i będzie walczył przeciwko tym narodom, tak jak wtedy, gdy walczył w dniu bitwy.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
I jego nogi staną w tym dniu na Górze Oliwnej, która [leży] naprzeciw Jerozolimy od strony wschodniej, a Góra Oliwna rozpadnie się na pół, na wschód i na zachód, [tworząc] wielką dolinę; i połowa tej góry cofnie się na północ, a połowa jej – na południe.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
Wtedy będziecie uciekać do doliny [tych] gór, bo dolina tych gór będzie sięgać aż do Azal. Będziecie uciekać, jak uciekaliście przed trzęsieniem ziemi za dni Uzjasza, króla Judy. Potem przyjdzie PAN, mój Bóg, [a] z nim wszyscy święci.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
A w tym dniu nie będzie wspaniałej światłości ani gęstej ciemności;
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
Lecz będzie to jeden dzień, który jest znany [tylko] PANU, nie [będzie] to dzień ani noc. A o wieczornej porze nastanie światło.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
W tym dniu wyjdą wody żywe z Jerozolimy; połowa ich do morza wschodniego, a połowa – do morza zachodniego. Będzie [to] w lecie i w zimie.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
A PAN będzie królem nad całą ziemią. W tym dniu jeden będzie PAN i jedno jego imię.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
Cała ziemia zamieni się w równinę od Geba aż do Rimmon, na południe od Jerozolimy. Będzie wywyższona i zamieszkana na swoim miejscu, od Bramy Beniamina aż do miejsca dawnej bramy i aż do Bramy Narożnej i od Wieży Chananeela aż do tłoczni królewskich.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
I będą w niej mieszkać, a nie będzie już przekleństwem. Jerozolima będzie zamieszkiwać w pokoju.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
A taka będzie plaga, którą PAN dotknie wszystkie narody, które walczyły przeciwko Jerozolimie: Ich ciała będą się rozkładać, gdy jeszcze będą stać na nogach, ich oczy będą gnić w oczodołach i ich język zgnije w ustach.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
W tym dniu będzie wśród nich wielkie zamieszanie od PANA, tak że jeden uchwyci rękę drugiego, a jego ręka podniesie się na rękę swego bliźniego.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
Juda także będzie walczyć w Jerozolimie, a bogactwa wszystkich narodów okolicznych będą zgromadzone: złoto, srebro i szaty w wielkiej ilości.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
A taka sama plaga jak tamta dotknie konie, muły, wielbłądy, osły oraz wszystkie zwierzęta, które będą w tym obozie.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
Wszyscy pozostali [spośród] wszystkich narodów, które wyruszyły przeciwko Jerozolimie, będą przychodzić od roku do roku, by oddawać pokłon Królowi, PANU zastępów, i obchodzić Święto Namiotów;
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
A jeśli ktoś spośród rodów ziemi nie pójdzie do Jerozolimy, by oddawać pokłon Królowi, PANU zastępów, na tego nie będzie [padać] deszcz.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
A jeśli ród Egiptu nie wyruszy i nie przyjdzie, choć na niego deszcz nie [pada], spadnie jednak [na niego ta] plaga, którą PAN dotknie narody, które nie przyjdą, by obchodzić Święto Namiotów.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
Taka będzie kara dla Egiptu i kara dla wszystkich narodów, które nie przychodzą na obchody Święta Namiotów.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
W tym dniu na dzwoneczkach koni będzie [taki napis]: Świętość PANU; a kotłów w domu PANA będzie jak czasz przed ołtarzem.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Każdy kocioł w Jerozolimie i Judzie będzie poświęcony PANU zastępów. Wszyscy, którzy składają ofiary, przyjdą i będą je brali, i będą w nich gotowali. W tym dniu nie będzie już Kananejczyka w domu PANA zastępów.

< Zekariya 14 >