< Zekariya 13 >

1 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
In that day every place shall be opened to the house of David and to the inhabitants of Jerusalem for removal and for separation.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
And it shall come to pass in that day, says the Lord of hosts, [that] I will utterly destroy the names of the idols from off the land, and there shall be no longer [any] remembrance of them: and I will cut off the false prophets and the evil spirit from the land.
3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
And it shall come to pass, if a man will yet prophesy, that his father and his mother which gave birth to him shall say to him, You shall not live; for you has spoken lies in the name of the Lord: and his father and his mother who gave him birth shall bind him as he is prophesying.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
And it shall come to pass in that day, [that] the prophets shall be ashamed every one of his vision when he prophesies; and they shall clothe themselves with a garment of hair, because they have lied.
5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
And [one] shall say, I am not a prophet, for I am a tiller of the ground, for a man brought me up [thus] from my youth.
6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
And I will say to him, What are these wounds between your hands? and he shall say, [Those] with which I was wounded in my beloved house.
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
Awake, O sword, against my shepherds, and against the man [who is] my citizen, says the Lord Almighty: strike the shepherds, and draw out the sheep: and I will bring mine hand upon the little ones.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
And it shall come to pass, [that] in all the land, says the Lord, two parts thereof shall be cut off and perish; but the third shall be left therein.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”
And I will bring the third [part] through the fire, and I will try them as silver is tried, and I will prove them as gold is proved: they shall call upon my name, and I will hear them, and say, This is my people: and they shall say, The Lord [is] my God.

< Zekariya 13 >