< Nyimbo ya Solomoni 8 >

1 Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga, amene anayamwa mawere a amayi anga! Ndikanakumana nawe pa njira, ndikanakupsompsona, ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.
I wish that you were like my brother, who nursed at my mother's breasts. Then whenever I met you outside, I could kiss you, and no one would despise me.
2 Ndikanakutenga ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, amayi amene anandiphunzitsa, ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe, zotsekemera za makangadza.
I would lead you and bring you into my mother's house— she who taught me. I would give you spiced wine to drink and some of the juice of my pomegranates.
3 Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.
His left hand is under my head and his right hand embraces me.
4 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani: musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
I want you to swear, daughters of Jerusalem, that you will not interrupt our lovemaking until it is over.
5 Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo, atatsamira wokondedwa wakeyo? Mkazi Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi, pamenepo ndi pamene amayi anachirira, pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.
Who is this who is coming up from the wilderness, leaning on her beloved? The woman speaking to the man I awakened you under the apricot tree; there your mother conceived you; there she gave birth to you, she delivered you.
6 Undiyike pamtima pako ngati chidindo, ngati chidindo cha pa dzanja lako; pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa, nsanje ndiyaliwuma ngati manda. Chikondi chimachita kuti lawilawi ngati malawi a moto wamphamvu. (Sheol h7585)
Set me as a seal over your heart, like a seal on your arm, for love is as strong as death. Passionate devotion is as unrelenting as Sheol; its flames burst out; it is a blazing flame, a flame hotter than any other fire. (Sheol h7585)
7 Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi, mitsinje singachikokolole chikondicho. Ngati wina apereka chuma chonse cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi, adzangonyozeka nazo kotheratu.
Surging waters cannot quench love, nor can floods sweep it away. If a man gave all the possessions in his house for love, the offer would utterly be despised.
8 Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono, koma alibe mawere, kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu pa tsiku limene adzamufunsire?
We have a little sister, and her breasts have not yet grown. What can we do for our sister on the day when she will be promised in marriage?
9 Ngati iye ndi khoma, tidzamumangira nsanja ya siliva. Ngati iye ndi chitseko, tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.
If she is a wall, we will build on her a tower of silver. If she is a door, we will adorn her with boards of cedar.
10 Ine ndili ngati khoma, ndipo mawere anga ndi nsanja zake. Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa ndine wobweretsa mtendere.
I was a wall, but my breasts are now like fortress towers; so I am in his eyes as one who brings peace.
11 Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni; iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi, aliyense mwa iwo ankayenera kupereka ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.
Solomon had a vineyard at Baal Hamon. He gave the vineyard to those who would maintain it. Each one was to bring a thousand shekels of silver for its fruit.
12 Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha. Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000 ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.
My vineyard, my very own, is before me; the thousand shekels are for you, Solomon, and the two hundred shekels are for those who maintain its fruit.
13 Iwe amene umakhala mʼminda uli pamodzi ndi anzako, ndilole kuti ndimve liwu lako!
You who live in the gardens, my companions are listening for your voice; let me hear it.
14 Fulumira wokondedwa wanga, ndipo ukhale ngati gwape kapena mwana wa mbawala wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.
Hurry, my beloved, and be like a gazelle or a young stag on the mountains of spices.

< Nyimbo ya Solomoni 8 >