< Nyimbo ya Solomoni 7 >

1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Kako su lijepe noge tvoje u obuæi, kæeri kneževska; sastavci su bedara tvojih kao grivne, djelo ruku umjetnièkih.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Pupak ti je kao èaša okrugla, koja nije nikad bez piæa; trbuh ti je kao stog pšenice ograðen ljiljanima;
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Dvije dojke tvoje kao dva blizanca srnèeta;
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Vrat ti je kao kula od slonove kosti; oèi su ti kao jezera u Esevonu na vratima Vatravimskim; nos ti je kao kula Livanska koja gleda prema Damasku;
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Glava je tvoja na tebi kao Karmil, i kosa na glavi tvojoj kao carska porfira u bore nabrana.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Kako si lijepa i kako si ljupka, o ljubavi u milinama!
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Uzrast ti je kao palma, i dojke kao grozdovi.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Rekoh: popeæu se na palmu, dohvatiæu grane njezine; i biæe dojke tvoje kao grozdovi na vinovoj lozi, i miris nosa tvojega kao jabuke;
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
I grlo tvoje kao dobro vino, koje ide pravo dragomu mojemu i èini da govore usne onijeh koji spavaju.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Ja sam dragoga svojega, i njega je želja za mnom.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Hodi, dragi moj, da idemo u polje, da noæujemo u selima.
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
Raniæemo u vinograde da vidimo cvate li vinova loza, zameæe li se grožðe, cvatu li šipci; ondje æu ti dati ljubav svoju.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Mandragore puštaju miris, i na vratima je našim svakojako krasno voæe, novo i staro, koje za te dohranih, dragi moj.

< Nyimbo ya Solomoni 7 >