< Nyimbo ya Solomoni 6 >

1 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti? Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
Kuda otide dragi tvoj, najljepša meðu ženama? kuda zamaèe dragi tvoj, da ga tražimo s tobom?
2 Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake, ku timinda ta zokometsera zakudya, akukadyetsa ziweto zake ku minda, ndiponso akuthyola maluwa okongola.
Dragi moj siðe u vrt svoj, k lijehama mirisnoga bilja, da pase po vrtovima i da bere ljiljane.
3 Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga; amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
Ja sam dragoga svojega, i moj je dragi moj, koji pase meðu ljiljanima.
4 Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
Lijepa si, draga moja, kao Tersa, krasna si kao Jerusalim, strašna kao vojska sa zastavama.
5 Usandipenyetsetse; pakuti maso ako amanditenga mtima. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Odvrati oèi svoje od mene, jer me raspaljuju. Kosa ti je kao stado koza koje se vide na Galadu.
6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa, iliyonse ili ndi ana amapasa, palibe imene ili yokha.
Zubi su ti kao stado ovaca kad izlaze iz kupala, koje se sve blizne a nijedne nema jalove.
7 Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu, masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
Jagodice su tvoje izmeðu vitica tvojih kao kriška šipka.
8 Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60, ndi azikazi 80, ndi anamwali osawerengeka;
Šezdeset ima carica i osamdeset inoèa, i djevojaka bez broja;
9 koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense; mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake, mwana wapamtima wa amene anamubereka. Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala; akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
Ali je jedna golubica moja, bezazlena moja, jedinica u matere svoje, izabrana u roditeljke svoje. Vidješe je djevojke i nazivaše je blaženom; i carice i inoèe hvališe je.
10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha, wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa, wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
Ko je ona što se vidi kao zora, lijepa kao mjesec, èista kao sunce, strašna kao vojska sa zastavama?
11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa, kukaona ngati mpesa waphukira kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
Siðoh u orašje da vidim voæe u dolu, da vidim cvate li vinova loza, pupe li šipci.
12 Ndisanazindikire kanthu, ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
Ne doznah ništa, a duša me moja posadi na kola Aminadavova.
13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami; bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe! Mwamuna Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami, pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
Vrati se, vrati se Sulamko, vrati se, vrati se, da te gledamo. Šta æete gledati na Sulamci? kao èete vojnièke.

< Nyimbo ya Solomoni 6 >