< Nyimbo ya Solomoni 5 >

1 Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
Wszedłem do mojego ogrodu, moja siostro, [moja] oblubienico. Zbierałem moją mirrę z moimi wonnościami; zjadłem mój plaster z moim miodem, piję moje wino z moim mlekiem. Jedzcie, przyjaciele, pijcie, a pijcie obficie, moi mili.
2 Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
Ja śpię, ale moje serce czuwa. [Oto] głos mego umiłowanego, który puka i [mówi]: Otwórz mi, moja siostro, moja umiłowana, moja gołębico, moja nieskalana. Moja głowa bowiem jest pełna rosy, moje kędziory – kropli nocy.
3 Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
Zdjęłam już swoją suknię, jakże mam ją wkładać? Umyłam swoje nogi, jakże mam je pobrudzić?
4 Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
Mój umiłowany wsunął swoją rękę przez otwór, a moje wnętrze poruszyło się we mnie.
5 Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
Wstałam, aby otworzyć mojemu umiłowanemu, a oto z moich rąk kapała mirra, z moich palców mirra spływała na uchwyt zasuwy.
6 Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
Otworzyłam mojemu umiłowanemu, lecz mój umiłowany [już] odszedł i zniknął. Moja dusza zasłabła na jego głos. Szukałam go, ale nie znalazłam, wołałam go, ale mi nie odpowiedział.
7 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
Znaleźli mnie strażnicy, którzy obchodzili miasto; pobili mnie i zranili, strażnicy murów zabrali mi zasłonę.
8 Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
Zaklinam was, córki Jerozolimy: Jeśli znajdziecie mojego umiłowanego, to powiedzcie mu, że jestem chora z miłości.
9 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
Czym przewyższa twój umiłowany [innych] umiłowanych, o najpiękniejsza wśród kobiet? Czym przewyższa twój umiłowany [innych] umiłowanych, że tak nas zaklinasz?
10 Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
Mój umiłowany jest biały i rumiany, i najznakomitszy spośród dziesięciu tysięcy.
11 Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
Jego głowa jest [jak] najczystsze złoto; jego kędziory faliste, czarne jak kruk.
12 Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
Jego oczy są jak gołębice nad strumieniami wody, [jakby] umyte w mleku, osadzone w swej oprawie.
13 Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
Jego policzki jak grządka wonności, [jak] pachnące kwiatki; jego wargi jak lilie ociekające wyborną mirrą.
14 Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
Jego ręce [jak] złote pierścienie wysadzone berylem; jego tors [jak] jasna kość słoniowa pokryta szafirem.
15 Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
Jego nogi [jak] słupy z marmuru, postawione na szczerozłotych podstawkach; jego oblicze [jak] Liban, wyborne jak cedry.
16 Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.
Jego usta przesłodkie i jest on cały przepiękny. Taki jest mój umiłowany i taki jest mój przyjaciel, córki Jerozolimy.

< Nyimbo ya Solomoni 5 >