< Nyimbo ya Solomoni 1 >

1 Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
Solomunova pjesma nad pjesmama.
2 Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
Da me hoæe poljubiti poljupcem usta svojih! Jer je tvoja ljubav bolja od vina.
3 Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
Mirisom su tvoja ulja prekrasna; ime ti je ulje razlito; zato te ljube djevojke.
4 Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
Vuci me, za tobom æemo trèati; uvede me car u ložnicu svoju; radovaæemo se i veseliæemo se tobom, spominjaæemo ljubav tvoju više nego vino; pravi ljube te.
5 Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
Crna sam, ali lijepa, kæeri Jerusalimske, kao šatori Kidarski, kao zavjesi Solomunovi.
6 Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
Ne gledajte me što sam crna, jer me je sunce opalilo; sinovi matere moje rasrdivši se na me postaviše me da èuvam vinograde, i ne èuvah svojega vinograda, koji ja imam.
7 Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
Kaži mi ti, kojega ljubi duša moja, gdje paseš, gdje planduješ? jer zašto bih lutala meðu stadima drugova tvojih?
8 Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
Ako ne znaš, najljepša izmeðu žena, poði tragom za stadom, i pasi jariæe svoje pokraj stanova pastirskih.
9 Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
Ti si mi, draga moja, kao konji u kolima Faraonovijem.
10 Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
Obrazi su tvoji okiæeni grivnama, i grlo tvoje nizovima.
11 Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
Naèiniæemo ti zlatne grivne sa šarama srebrnijem.
12 Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
Dok je car za stolom, narad moj pušta svoj miris.
13 Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
Dragi mi je moj kita smirne, koja meðu dojkama mojim poèiva.
14 Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
Dragi mi je moj grozd kiprov iz vinograda Engadskih.
15 Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
Lijepa ti si, draga moja, lijepa ti si! oèi su ti kao u golubice.
16 Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
Lijep ti si, dragi moj, i ljubak! i postelja naša zeleni se.
17 Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.
Grede su nam u kuæama kedrove, daske su nam jelove.

< Nyimbo ya Solomoni 1 >