< Rute 2 >

1 Naomi anali ndi mʼbale wake wolemera kwambiri wochokera ku banja la mwamuna wake Elimeleki, dzina lake Bowazi.
A bijaše jedan èovjek, rod mužu Nojemininu, èovjek bogat od porodice Elimelehove, kojemu ime bijaše Voz.
2 Tsiku lina Rute, Mmowabu uja anati kwa Naomi, “Mundilole kuti ndikakunkhe barele ku munda wa munthu aliyense amene akandikomere mtima.” Naomi anati kwa iye, “Pita mwana wanga.”
I Ruta Moavka reèe Nojemini: da idem u polje da pabirèim klasje za onijem pred kim naðem milost. A ona joj reèe: idi, kæeri moja.
3 Choncho Rute ananyamuka kupita kukakunkha ku minda yokololedwa kale. Tsono zinangochitika kuti Rute anafika mʼmunda wa Bowazi, yemwe anali wochokera ku banja la Elimeleki.
I ona otide, i došavši stade pabirèiti po njivi za žeteocima: i dogodi se, te doðe na njivu koja pripadaše Vozu, koji bijaše od porodice Elimelehove.
4 Posakhalitsa Bowazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okolola aja kuti, “Yehova akhale nanu!” Iwo anayankha kuti, “Yehova akudalitseni.”
I gle, doðe Voz iz Vitlejema, i reèe žeteocima: Gospod da je s vama! I oni mu rekoše: da te blagoslovi Gospod!
5 Bowazi anafunsa kapitawo wake amene ankayangʼanira okolola aja kuti, “Mayi uyo ndi ndani?”
Tada reèe Voz sluzi svojemu koji bijaše nad žeteocima: èija je ona mladica?
6 Kapitawo uja anayankha kuti, “Mayiyu ndi Mmowabu amene anabwera ndi Naomi kuchokera ku dziko la Mowabu.
A sluga koji bješe nad žeteocima odgovori mu: Moavka je mladica koja se vratila s Nojeminom iz zemlje Moavske.
7 Iye anandipempha kuti, ‘Chonde mundilole kuti ndikunkhe barele mʼminda moti akololamo kale.’ Iye wakhala akukunkha kuyambira mmawa mpaka tsopano lino osapuma nʼpangʼono pomwe.”
I reèe: da pabirèim, da kupim klasje izmeðu snopova za žeteocima. I došavši bavi se od jutra do sada; samo je malo bila kod kuæe.
8 Choncho Bowazi anati kwa Rute, “Tamvera mwana wanga, usapite kukakunkha mʼmunda wina, ndipo usachoke mʼmunda uno. Koma uzitsata adzakazi angawa.
Tada Voz reèe Ruti: èuješ, kæeri moja; nemoj iæi na drugu njivu da pabirèiš, niti odlazi odavde, nego se drži mojih djevojaka.
9 Uziyangʼana munda akukolola anyamatawo akamakolola mʼmundamu, ndipo iwe uzitsata pambuyo pawo. Ndawawuza anyamatawo kuti asakuvutitse. Ndipo ukamva ludzu, uzipita ku mitsuko ndi kukamwa madzi amene anyamatawa atunga.”
Pazi na kojoj njivi oni žanju, pa idi za njima; jer sam zapovjedio momcima svojim da te niko ne dira; a kad ožedniš, idi k sudovima i pij što moje sluge zahitaju.
10 Atamva zimenezi Rute anawerama nazolikitsa nkhope yake pansi. Kenaka anafunsa kuti, “Mwandikomera mtima chotere mlendo ngati ine chifukwa chiyani?”
Tada ona pade nièice i pokloni se do zemlje, i reèe mu: kako naðoh milost pred tobom, da me pogledaš, kad sam tuðinka?
11 Bowazi anayankha kuti, “Ine ndawuzidwa zonse zimene wakhala ukuchitira apongozi ako chimwalirire mwamuna wako. Ndamvanso kuti unasiya abambo ndi amayi ako komanso dziko la kwanu ndi kubwera kudzakhala ndi anthu amene sumawadziwa ndi kale lonse.
A Voz odgovori i reèe joj: èuo sam ja sve što si èinila svekrvi svojoj po smrti muža svojega, i kako si ostavila oca svojega i mater svoju i postojbinu svoju, pa si došla k narodu kojega nijesi znala prije.
12 Yehova akubwezere pa zimene wachitazi. Yehova Mulungu wa Israeli, amene wabwera pansi pa mapiko ake kuti akuteteze, akupatse mphotho yayikulu.”
Gospod da ti plati za djelo tvoje, i da ti plata bude potpuna od Gospoda Boga Izrailjeva, kad si došla da se pod krilima njegovijem skloniš.
13 Rute anati, “Mwandikomera mtima, mbuye wanga. Ndipo mwandisangalatsa ndi kundiyankhula mwa chifundo ngakhale sindili mmodzi mwa adzakazi anu.”
A ona reèe: naðoh milost pred tobom, gospodaru, jer si me utješio i milostivo progovorio sluškinji svojoj, ako i nijesam kao jedna od tvojih sluškinja.
14 Nthawi ya chakudya cha masana Bowazi anati kwa iye, “Bwera kuno, utenge buledi ndi kusunsa nthongo mu vinyo.” Choncho anakhala pansi pafupi ndi okololawo, ndipo Bowazi anamupatsa chakudya ndi nyama yowotcha. Anadya chilichonse amafuna ndipo chakudya china chinatsalako.
A Voz joj reèe: kad bude vrijeme jesti, doði ovamo i jedi hljeba i umoèi zalogaj svoj u ocat. I ona sjede pokraj žetelaca, i on joj pruži prženijeh zrna, i ona jede i nasiti se, i preteèe joj.
15 Atanyamuka kuti azikakunkha, Bowazi analangiza anyamata ake kuti, “Ngakhale mayiyu azikunkha pakati pa mitolo musamuletse ndi kumuchititsa manyazi.
Potom usta da pabirèi. A Voz zapovjedi momcima svojim govoreæi: neka pabirèi i meðu snopovima, nemojte da je zastidite.
16 Koma muzimusololerako ngala zina za mʼmitolo ndi kumusiyira kuti azikunkha ndipo musamukalipire.”
Nego još navlaš ispuštajte rukoveti i ostavljajte joj neka kupi, i ne korite je.
17 Choncho Rute anakunkha mʼmundamo mpaka madzulo. Kenaka anapuntha barele anakunkhayo, ndipo anakwanira pafupifupi makilogalamu khumi.
I ona pabirèi na njivi do veèera, i ovrše što napabirèi, i doðe oko efe jeèma.
18 Anasenza barele uja kupita naye ku mudzi, nakaonetsa apongozi ake. Kenaka anatulutsa chakudya chimene chinatsalira atakhuta chija ndi kupatsa apongozi ake.
I uzevši otide u grad, i vidje svekrva njezina šta je napabirèila; a ona izvadi i dade joj i ono što joj je preteklo pošto se nasitila.
19 Apongozi akewo anamufunsa kuti, “Kodi lero unakakunkha kuti? Unakagwira kuti ntchitoyi? Adalitsike munthu amene anakukomera mtimayo.” Ndipo Rute anawuza mpongozi wake za munthu amene ku malo ake anakagwirako ntchito. Iye anati, “Munthuyo dzina lake ndi Bowazi.”
I reèe joj svekrva: gdje si pabirèila danas? i gdje si radila? Da je blagosloven koji te je pogledao! A ona kaza svekrvi svojoj kod koga je radila govoreæi: ime je èovjeku kod kojega sam danas radila Voz.
20 Naomi anati kwa mpongozi wakeyo, “Munthu ameneyu amudalitse Yehova, amene sanasiye kuchitira chifundo anthu amoyo ndi akufa omwe. Anatinso munthu ameneyu ndi mnansi wapaphata. Ndiye ali ndi udindo wotisamalira.”
A Nojemina reèe snasi svojoj: Gospod da ga blagoslovi, kad nije ukratio milosti svoje k živima i k mrtvima. I reèe joj Nojemina: taj je èovjek nama rod, i jedan od osvetnika naših.
21 Choncho Rute Mmowabuyo anati, “Iye anandiwuzanso kuti, ‘Uzitsata antchito angawa mpaka atamaliza kukolola munda wonse.’”
A Ruta Moavka reèe: još mi je rekao: drži se moje èeljadi dokle ne požanju sve moje.
22 Naomi anati kwa Rute mpongozi wake, “Kuli bwino mwana wanga kuti uzipita ndi adzakazi ake kuopa kuti mʼmunda wa munthu wina angakuvute.”
A Nojemina reèe Ruti snasi svojoj: dobro je, kæeri moja, da ideš s njegovijem djevojkama, da te ne bi dirali na drugoj njivi.
23 Choncho Rute ankatsatira adzakazi a Bowazi namakunkha mpaka anthu atamaliza kudula barele ndi tirigu. Ndipo amakhalabe ndi mpongozi wakeyo.
I tako se držaše djevojaka Vozovijeh pabirèeæi dokle se ne svrši žetva jeèmena i žetva pšenièna; i življaše kod svekrve svoje.

< Rute 2 >