< Aroma 2 >

1 Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
Cedawngawh, nangmih, thlang awi ak dengkhqi, na mimah awm ap cang lawk uhyk ti, thlang awi nami dengnaak ahoei awh, namah ni na thawlh khqoeng hy, thlang awi ak deng nang ingawm cemyih ni na sai lawt hy.
2 Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
Cemyih them ak saikhqi ak khanawh Khawsa ak awidengnaak taw awitak awh ni ang dyih hy tice ni sim uhy.
3 Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
Cedawngawh, nang thlanghqing, namah ing cemyih ik-oeih ce na sai lawt dawngawh thlang awi na deng awh, Khawsa ak awidengnaak khui awhkawng loet tloe kawng nyng, tinawh nak poek nawh nu?
4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
Am awhtaw Khawsam qeennaak ing zutnaak benna ni sawi hy tice a sim kaana, am qeennaak, qeenkhaw ang ngainaak ingkaw ang yh thainaakkhqi ce kawna a huh kaana na awm nawh nu?
5 Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
Cehlai namik kawlung a hqamnaak ingkaw am nang zutnaakkhqi boeih ce, amah ak awidengnaak ak dyng khawnghi a pha awh, namah aham Khawsa ak kawsonaak ak cun nani na awm khqoeng hy.
6 Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
Khawsa ing thlang boeih ing ami them sainaak amyihna a phu ce pe kaw.
7 Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
Them leek sainaak a qoeng kaana boeimangnaak, kqihchah naak ingkaw amak see thai ik-oeih ak suikhqi venawh Khawsa ing kumqui hqingnaak ce pe kaw. (aiōnios g166)
8 Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
Cehlai amah ak kawngaih doeng sui nawh awitak ak oelhkhqi ingkaw them che ak sai thlangkhqi ham kawsonaak ce awm kaw:
9 Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Ik-oeih che ak sai thlangkhqi ham kawseetnaak ingkaw khuikhanaak awm kaw: Judakhqi aham awm maa kawmsaw cekcoengawh Gentelkhqi aham awm kaw;
10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
Cehlai boeimangnaak, kqihchahnaak ingkaw ngaihdingnaak ce ik-oeih leek ak saikhqi ham awm kaw: Judakhqi ham awm maa kawmsaw cekcoengawh Gentelkhqi ham awm kaw.
11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.
Ikawtih Khawsa ing u a haai awm am toek hy.
12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
Anaa awi kaana thawlhnaak ak saikhqi boeih taw anaa awi kaana plawci lawt kawm uh, anaa awi ak khuiawh thawlhnaak ak saikhqi boeih awm anaa awi ing awi deng lawt kaw.
13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
Ikawtih anaa awi ak zakhqi taw Khawsa haiawh thlak dyng na am awm hy, cehlai anaa awi haiawh thlak dyng na am ta pai hlai uhy,
14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
(Gentelkhqi ing Anaa awi ce am ta pai hlai uhy, a mimah poek awh anaa awi ing a ngoekhqi ce sai uhy, anaa awi am ta hlai uhy, cekkhqi aham anaa awi na awm hawh hy,
15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
anaa awi ing a ngoekhqi ce amik kawlung khuiawh qee hyt na awm hawh hy, a mimah a sim naak ingawm dyih pyi hy, amik poeknaak khqi ing thawlh puk unawh ang dyih na awm dyih pyi bai uhy.)
16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
Khawsa ing Jesu Khrih ak caming kai ing awithang leek kak khypyinaak amyihna thlanghqing awhkaw ang hyp kawpoekkhqi ce awi a deng awh ve ve awm bit kaw.
17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
Tuh nangmih ing, Juda thlang na awm unyng ti uhyk ti; anaa awi awh hang unawh Khawsa mi tuqunaak awh nang oek qu awhtaw;
18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
amah ak kawngaih ce sim u tiksaw anaa awi ing a ni cawngpyi amyihna ak leek khqoet ik-oeih ce nami sim awhtaw;
19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
mik hyp ak sawikung, thannaak ak khuiawh ak awmkhqi ham vangnaak na nami awm awhtaw;
20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
thlakqawkhqi lam ak huhkung, naasenkhqi ak cawngpyikung na ngai qu u tiksaw, anaa awi awhkawng cyihnaak ingkaw awitak ce ta hawh uhyk ti.
21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
Cawhtaw, nangmih, thlak chang ak cawngpyikungkhqi, namah ingkaw namah taw am nang cawng qu pyi nawh nu? Amamim quuknaak aham ak cawngpyikungkhqi ing namim qu nawh nu?
22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
Thlang ing a samphaih aham am awm hy tinawh ak kqawnkung ing, na sam na phaih nawh nu? Myiqawl bawknaak ak tyih nang ing, myiqawl bawknaak bawkimkhqi ce na muk nawh nu?
23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
Anaa awi ak oek qu pyikhqi ing, anaa awi eeknaak ing Khawsa ce nak thekhanaak nu?
24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
Nangmih awh Gentelkhqi anglakawh Khawsa'ng ming kqawn seet na awm hawh hy,” tinawh a qee amyihna.
25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
Anaa awi nami hquut awhtaw chahhui qeet ve phu tahy, cehlai anaa awi ce nami eek awhtaw, chahhui amak qeet thlang amih nani nami awm hy.
26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
Chahhui amak qeet thlangkhqi ing anaa awi ing a ngoe ce a mi hquut awhtaw, chahhui ak qeet thlang amyihna am nik poek kawm nu?
27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
Pumsa awh chahhui am qeet hlai hy anaa awi ak hquut ing nangmih ce ni thawlh sak khqi kaw, ca ing a qee anaa awi ta unawh chahhui ak qeet thlang na awm hlai uhyk ti, anaa awi ak eekkung na awm uhyk ti.
28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
Ak khanben doeng ak dang ingkaw ak khan benawh pumsa chahhui ak qeet doek ak thlang ce Juda thlang amni.
29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.
Ak khui benawh ak awm; Myihla ingkaw lingbyi kawlung chahui ak qeet ak thlang, ca doeng ing qee doek na amak awm ak thlang ce ni Juda thlang na a awm hy. Cemyih ak thlang ce thlanghqing ing am kyih pai hlai hy Khawsa ing kyih hy.

< Aroma 2 >