< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Śpiewajcie PANU nową pieśń, śpiewaj PANU, cała ziemio!
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Śpiewajcie PANU, błogosławcie jego imię, opowiadajcie o jego zbawieniu dzień po dniu.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Głoście wśród narodów jego chwałę, wśród wszystkich ludów jego cuda.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Wielki bowiem jest PAN i godny wszelkiej chwały, straszliwszy nad wszystkich bogów.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Gdyż wszyscy bogowie narodów [są] bożkami, a PAN uczynił niebiosa.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Cześć i majestat przed jego obliczem, moc i piękno w jego świątyni.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Oddajcie PANU, rodziny narodów, oddajcie PANU chwałę i moc.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Oddajcie PANU chwałę jego imienia, przynieście dary i wejdźcie do jego przedsionków.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Oddajcie PANU pokłon w ozdobie świętości, niech cała ziemia drży przed nim.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Mówcie wśród pogan: PAN króluje; świat będzie utwierdzony, aby się nie poruszył, i [on] będzie sądził ludzi sprawiedliwie.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Niech się weselą niebiosa i niech raduje się ziemia; niech zaszumi morze i to, co w nim jest.
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Niech radują się pola i wszystko, co jest na nich, wtedy [radośnie] wykrzykną wszystkie drzewa leśne;
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Przed obliczem PANA, bo idzie, zaprawdę idzie, aby sądzić ziemię. Będzie sądził świat w sprawiedliwości, a narody w swojej prawdzie.

< Masalimo 96 >