< Masalimo 88 >

1 Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
A song, a psalm of the sons of Korah; for the chief musician; set to the Mahalath Leannoth style. A maschil of Heman the Ezrahite. Yahweh, God of my salvation, I cry out day and night before you.
2 Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
Listen to my prayer; pay attention to my cry.
3 Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
For I am filled with troubles, and my life has reached Sheol. (Sheol h7585)
4 Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
People treat me like those who go down into the pit; I am a man with no strength.
5 Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
I am abandoned among the dead; I am like the dead who lie in the grave, about whom you care no more because they are cut off from your power.
6 Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
You place me in the lowest part of the pit, in the dark and deep places.
7 Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
Your wrath lies heavy on me, and all your waves crash over me. (Selah)
8 Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
Because of you, my acquaintances avoid me. You have made me a shocking sight to them. I am hemmed in and I cannot escape.
9 maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
My eyes grow weary from trouble; All day long I call out to you, Yahweh; I spread out my hands to you.
10 Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
Will you do wonders for the dead? Will those who have died rise and praise you? (Selah)
11 Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
Will your covenant faithfulness be proclaimed in the grave, your loyalty in the place of the dead?
12 Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
Will your wonderful deeds be known in the darkness, or your righteousness in the place of forgetfulness?
13 Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
But I cry to you, Yahweh; in the morning my prayer comes before you.
14 Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
Yahweh, why do you reject me? Why do you hide your face from me?
15 Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
I have always been afflicted and on the verge of death since my youth. I have suffered from your terrors; I am in despair.
16 Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
Your angry actions have passed over me, and your terrifying deeds have annihilated me.
17 Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
They surround me like water all the day long; they have all encircled me.
18 Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.
You have removed every friend and acquaintance from me. My only acquaintance is the darkness.

< Masalimo 88 >