< Masalimo 85 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
Smilovao si se, Gospode, na zemlju svoju, povratio si roblje Jakovljevo.
2 Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
Prostio si nepravdu narodu svojemu, pokrio si sve grijehe njegove.
3 Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
Ustavio si svu jarost svoju, ublažio žestinu gnjeva svojega.
4 Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
Povrati nas, Bože spasitelju naš, prekini srdnju svoju na nas.
5 Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
Zar æeš se dovijeka gnjeviti na nas, i protegnuti gnjev svoj od koljena na koljeno?
6 Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
Zar se neæeš povratiti i oživiti nas, da bi se narod tvoj radovao o tebi?
7 Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
Pokaži nam, Gospode, milost svoju, i pomoæ svoju daj nam.
8 Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
Da poslušam što govori Gospod Bog. On izrièe mir narodu svojemu i svecima svojim, i onima koji se obraæaju srcem k njemu.
9 Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
Da, blizu je onijeh koji ga se boje pomoæ njegova, da bi naselio slavu u zemlji našoj!
10 Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
Milost i istina srešæe se, pravda i mir poljubiæe se.
11 Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
Istina æe niknuti iz zemlje i pravda æe s neba priniknuti.
12 Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
I Gospod æe dati dobro, i zemlja naša daæe plod svoj.
13 Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.
Pravda æe pred njim iæi, i postaviæe na put stope svoje.

< Masalimo 85 >