< Masalimo 83 >

1 Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Pesem in psalm Asafu. O Bog, ne molči, ne delaj se gluhega, in ne mirúj, o Bog mogočni!
2 Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Ker glej, neprijatelji tvoji ropotajo, in sovražniki tvoji dvigujejo glavo.
3 Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Zoper ljudstvo tvoje prekanjeno delajo naklep; in posvetujejo se zoper skrite tvoje.
4 Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
Rekoč: Dejte, potrebimo jih, da ne bodejo narod, da se ne bode več imenovalo ime Izraelovo.
5 Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Ker naklep so storili z enakimi srci; zoper tebe so sklenili zavezo.
6 Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
Šatori Idumejcev in Izmaeličanov, Moabljani in Agarenci;
7 Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Gebaljani in Amonjani in Amalečani; Palestinjani s Tira prebivalci.
8 Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
Tudi Asirijan se jim je pridružil; roka so sinovom Lotovim.
9 Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
Stóri jim kakor Madijanom, kakor Sisaru, kakor Jabinu ob potoku Kisonu,
10 Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
Ki so bili pokončani pri Endoru; postali so zemlje gnoj.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
Naredi njih plemenitnike same kakor Oreba, in kakor Zeba; kakor Zebaha in Salmuna vse njih poglavarje,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
Kateri pravijo: Pridobimo prebivališča Božja.
13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
Bog moj, naredi jih kakor kolo, kakor pleve pred vetrom.
14 Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
Kakor ogenj požiga gozd, in kakor plamen vnema gore,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
Tako jih pódi z viharjem svojim; in z vrtincem svojim jih preplaši.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
Sè sramoto napolni njih obličje; da se bode iskalo ime tvoje, o Gospod.
17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
Rudečica naj jih oblije, in zbegajo naj se večno; sramujejo se naj in poginejo;
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.
Da se spozná, da si ti, kateremu edinemu je ime Gospod, vzvišen nad vesoljno zemljo.

< Masalimo 83 >