< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Przewodnikowi chóru, na Gittyt. Asafa. Radośnie śpiewajcie Bogu, naszej mocy; [radośnie] wykrzykujcie Bogu Jakuba.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Weźcie psalm, przynieście bęben, wdzięczną harfę i cytrę.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Zadmijcie w trąbę w czas nowiu, w czasie wyznaczonym, w dniu naszego uroczystego święta.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Jest bowiem taki nakaz w Izraelu, prawo Boga Jakuba.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Ustanowił to świadectwem dla Józefa, kiedy wyszedł przeciw ziemi Egiptu, gdzie słyszałem język, którego nie zrozumiałem.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
Uwolniłem od brzemienia jego barki, a jego ręce od [dźwigania] kotłów.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Wzywałeś mnie w ucisku i wybawiłem cię; odpowiedziałem ci w skrytości gromu, doświadczyłem cię u wód Meriba. (Sela)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Słuchaj, mój ludu, a oświadczę ci; Izraelu, jeśli będziesz mnie słuchał;
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Nie będziesz miał cudzego boga ani nie oddasz pokłonu obcemu bogu;
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Ja, PAN, [jestem] twoim Bogiem, który cię wyprowadził z ziemi Egiptu; otwórz usta, a ja je napełnię.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Lecz mój lud nie usłuchał mego głosu, a Izrael nie chciał mnie.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Zostawiłem ich więc żądzom ich serca i postępowali według swoich zamysłów.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
O, gdyby mój lud mnie posłuchał, a Izrael chodził moimi drogami!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
W krótkim czasie poniżyłbym ich nieprzyjaciół i zwróciłbym rękę przeciw ich wrogom.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Nienawidzący PANA, choć obłudnie, musieliby mu się poddać, a ich czas trwałby wiecznie.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
I karmiłbym ich wyborną pszenicą, a nasyciłbym cię miodem ze skały.

< Masalimo 81 >