< Masalimo 81 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
To the ouercomer in the pressours of Asaph. Make ye fulli ioye to God, oure helpere; synge ye hertli to God of Jacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Take ye a salm, and yyue ye a tympan; a myrie sautere with an harpe.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blowe ye with a trumpe in Neomenye; in the noble dai of youre solempnite.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For whi comaundement is in Israel; and doom is to God of Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He settide that witnessing in Joseph; whanne he yede out of the lond of Egipt, he herde a langage, which he knew not.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
He turnede a wei his bak fro birthens; hise hondis serueden in a coffyn.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
In tribulacioun thou inwardli clepidist me, and Y delyuerede thee; Y herde thee in the hid place of tempest, Y preuede thee at the water of ayenseiyng.
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
My puple, here thou, and Y schal be witnesse ayens thee;
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Israel, if thou herist me, a fresche God schal not be in thee, and thou schalt not worschipe an alien god.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
For Y am thi Lord God, that ladde thee out of the lond of Egipt; make large thi mouth, and Y schal fille it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
And my puple herde not my vois; and Israel yaue not tente to me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
And Y lefte hem aftir the desiris of her herte; thei schulen go in her fyndyngis.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
If my puple hadde herde me; if Israel hadde go in my weies.
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
For nouyt in hap Y hadde maad low her enemyes; and Y hadde send myn hond on men doynge tribulacioun to hem.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The enemyes of the Lord lieden to hym; and her tyme schal be in to worldis.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
And he fedde hem of the fatnesse of whete; and he fillide hem with hony of the stoon.

< Masalimo 81 >