< Masalimo 80 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
Pastire Izrailjev, èuj! koji vodiš sinove Josifove kao ovce, koji sjediš na heruvimima, javi se!
2 kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
Pred Jefremom i Venijaminom i Manasijom probudi krjepost svoju, i hodi da nam pomožeš.
3 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Bože! povrati nas, neka zasja lice tvoje da se spasemo!
4 Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Gospode, Bože nad vojskama! dokle æeš se gnjeviti kad te moli narod tvoj?
5 Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Hraniš ih hljebom suznijem, i pojiš ih suzama trostrukom mjerom.
6 Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
Uèinio si da se oko nas svaðaju susjedi naši, i neprijatelji se naši smiju meðu sobom.
7 Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Bože nad vojskama! povrati nas, neka zasja lice tvoje da se spasemo!
8 Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Iz Misira si prenio èokot, izagnao narode, i posadio ga.
9 Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
Okrèio si za nj, i on pusti žile, i zauze svu zemlju.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
Gore se pokriše njegovijem sjenom, i loze su mu kao kedri Božiji.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
Pustio je loze svoje do mora i ogranke svoje do rijeke.
12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
Zašto si mu razvalio ogradu, da ga kida ko god proðe?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
Gorski vepar podgriza ga, i poljska zvijer jede ga.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
Bože nad vojskama! obrati se, pogledaj s neba i vidi, i obiði vinograd ovaj,
15 muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
Sad ovaj, koji je posadila desnica tvoja, i sina, kojega si ukrijepio sebi!
16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
Popaljen je ognjem, isjeèen, od strašnoga pogleda tvojega propade.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
Neka bude ruka tvoja nad èovjekom desnice tvoje, nad sinom èovjeèijim kojega si utvrdio sebi!
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
I neæemo otstupiti od tebe, oživi nas, i ime tvoje prizivaæemo.
19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
Gospode, Bože nad vojskama! povrati nas, neka zasja lice tvoje, da se spasemo!

< Masalimo 80 >