< Masalimo 79 >

1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Psalm Asafa. Boże, poganie wtargnęli do twego dziedzictwa, splugawili twoją świętą świątynię, Jeruzalem zamienili w ruiny.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
Zwłoki twoich sług dali na żer ptactwu niebieskiemu, ciała twoich świętych bestiom ziemskim.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
Rozlali ich krew jak wodę wokół Jeruzalem i nie było nikogo, kto by ich pogrzebał.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
Staliśmy się hańbą dla naszych sąsiadów, pośmiewiskiem i drwiną dla tych, którzy są wokoło nas.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Jak długo, PANIE? Czy wiecznie będziesz się gniewać? Czy twoja zapalczywość będzie płonąć jak ogień?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Wylej twój gniew na pogan, którzy cię nie znają, i na królestwa, które nie wzywają twego imienia.
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
Pożarli bowiem Jakuba i spustoszyli jego mieszkanie.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Nie pamiętaj nam dawnych nieprawości naszych, niech nas prędko spotka twoje miłosierdzie, bo jesteśmy bardzo wynędzniali.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Wspomóż nas, Boże naszego zbawienia, dla chwały imienia twego; ocal nas i przebacz nam grzechy ze względu na twoje imię.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Dlaczego poganie mają mówić: Gdzież jest ich Bóg? Niech będzie znany wśród pogan na naszych oczach przez dokonanie zemsty za przelaną krew twoich sług.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Niech dotrze do ciebie jęk więźniów, według potęgi twego ramienia zachowaj skazanych na śmierć.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
I odpłać naszym sąsiadom siedmiokrotnie w ich zanadrze za zniewagę, którą ci wyrządzili, Panie!
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
My zaś, twój lud i owce twego pastwiska, będziemy cię wielbić na wieki, będziemy głosić twoją chwałę z pokolenia na pokolenie.

< Masalimo 79 >