< Masalimo 79 >

1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
A psalm of Asaph. God, foreign nations have come into your inheritance; they have defiled your holy temple; they have turned Jerusalem into a heap of ruins.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
They have given the dead bodies of your servants as food to the birds of the skies, the bodies of your faithful people to the beasts of the earth.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
They have shed their blood like water around Jerusalem, and there was none to bury them.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
We have become a reproach for our neighbors, mocking and derision to those who are around us.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
How long, Yahweh? Will you stay angry forever? How long will your jealous anger burn like fire?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Pour out your wrath on the nations that do not know you and on the kingdoms that do not call upon your name.
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
For they have devoured Jacob and destroyed his villages.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Do not hold the sins of our forefathers against us; may your merciful actions come to us, for we are very low.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Help us, God of our salvation, for the sake of the glory of your name; save us and forgive our sins for your name's sake.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Why should the nations say, “Where is their God?” May the blood of your servants that was shed be avenged on the nations before our eyes.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
May the groans of the prisoners come before you; with the greatness of your power keep the children of death alive.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
Pay back into the laps of our neighboring countries seven times as much as the insults with which they have insulted you, Lord.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
So we your people and sheep of your pasture will give you thanks forever. We will tell your praises to all generations.

< Masalimo 79 >