< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Pieśń pouczająca. Asafa. Słuchaj, mój ludu, mego prawa, nakłońcie uszu ku słowom moich ust.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
Otworzę moje usta do przypowieści, opowiem starodawne tajemnice;
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Cośmy słyszeli i poznali i [co] nam opowiadali nasi ojcowie.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Nie zataimy [tego] przed ich synami, opowiemy przyszłemu pokoleniu o chwale PANA, o jego mocy i cudach, które czynił.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
Ustanowił bowiem świadectwo w Jakubie, nadał prawo w Izraelu i nakazał naszym ojcom, aby je oznajmiali swoim synom;
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Aby poznało przyszłe pokolenie, synowie, którzy się urodzą; aby powstawszy, przekazywali [je] swoim synom;
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
Żeby pokładali w Bogu nadzieję i nie zapominali o dziełach Boga, lecz strzegli jego przykazań;
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
Żeby nie byli, jak ich ojcowie, pokoleniem opornym i nieposłusznym; pokoleniem, które nie przygotowało swego serca i którego duch nie był wierny Bogu.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Synowie Efraima, uzbrojeni i wyposażeni w łuki, w dniu bitwy wycofali się.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
[Bo] nie strzegli przymierza Boga i nie chcieli postępować według jego prawa.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
Zapomnieli o jego dziełach i cudach, które im ukazał.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Przed ich ojcami czynił cuda w ziemi Egiptu, na polu Soanu.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Rozdzielił morze i przeprowadził ich, i sprawił, że wody stanęły jak wał.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
Prowadził ich w obłoku za dnia, a całą noc w blasku ognia.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
Rozszczepił skały na pustyni i napoił ich jakby z wielkich głębin.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
Wydobył strumienie ze skały i sprawił, że wody płynęły jak rzeki.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Lecz [oni] jeszcze więcej grzeszyli przeciwko niemu i pobudzili do gniewu Najwyższego na pustyni;
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
I wystawiali Boga na próbę w swych sercach, żądając pokarmu według swego pragnienia.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
I mówili przeciwko Bogu tymi słowy: Czy Bóg może zastawić stół na tej pustyni?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Oto uderzył w skałę i wypłynęły wody, i wezbrały strumienie; czy będzie mógł też dać chleb? Czy przygotuje mięso swemu ludowi?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Gdy PAN [to] usłyszał, rozgniewał się i ogień zapłonął przeciw Jakubowi, i gniew wybuchnął przeciw Izraelowi;
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Bo nie uwierzyli Bogu i nie zaufali jego zbawieniu;
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Choć rozkazał chmurom w górze i bramy nieba otworzył.
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
I zesłał im [jak] deszcz mannę do jedzenia, i zboże z nieba im dał.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Człowiek jadł chleb anielski; zesłał im pokarm do syta.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Wzbudził na niebie wiatr ze wschodu i sprowadził swą mocą wiatr południowy.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Zesłał im mięso jak pył i ptactwo skrzydlate jak piasek morski.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
Spadło ono pośrodku ich obozu, wokół ich namiotów.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
Jedli i w pełni się nasycili; dał im, czego pragnęli.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
[A gdy] jeszcze nie zaspokoili swego pragnienia, [gdy] jeszcze pokarm był w ich ustach;
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
Spadł na nich gniew Boży i zabił ich tłustych, a znakomitszych z Izraela powalił.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Mimo to nadal grzeszyli i nie wierzyli jego cudom;
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Dlatego sprawił, że ich dni przemijały w marności, a ich lata – w trwodze.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Gdy ich zabijał, szukali go; nawracali się i o świcie szukali Boga;
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
Przypominali sobie, że Bóg [jest] ich skałą, że Bóg Najwyższy – ich Odkupicielem;
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
Pochlebiali mu jednak swoimi ustami i okłamywali go swym językiem;
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
A ich serce nie było przed nim szczere i nie byli wierni jego przymierzu.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
On jednak, będąc miłosiernym, przebaczał ich nieprawości i nie wytracał [ich]; często odwracał swój gniew i nie pobudzał całej swej zapalczywości;
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
Bo pamiętał, że są ciałem; wiatrem, który ulatuje i nie wraca.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Jak często pobudzali go do gniewu na pustyni [i] zasmucali go na pustkowiu!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Odwracali się i wystawiali Boga na próbę, i stawiali granice Świętemu Izraela.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Nie pamiętali jego ręki [ani] dnia, w którym ich wybawił z utrapienia;
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
Gdy czynił swe znaki w Egipcie i swe cuda na polu Soanu;
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
Gdy zamienił w krew ich rzeki i ich strumienie, tak że nie mogli [z nich] pić.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
Zesłał na nich rozmaite muchy, aby ich kąsały, i żaby, aby ich niszczyły;
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
I dał robactwu ich plony, a ich pracę szarańczy.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
Zniszczył gradem ich winorośle, a sykomory szronem.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
Ich bydło wydał na pastwę gradu, a ich stada [na pastwę] błyskawic.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
Wylał na nich żar swojego gniewu, zapalczywość, oburzenie i udrękę, zesławszy na nich złych aniołów.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
Otworzył drogę dla swego gniewu, nie zachował ich duszy od śmierci, a ich życie wydał zarazie;
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
Wytracił wszystko pierworodne w Egipcie, pierwociny [ich] mocy w namiotach Chama;
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
Ale swój lud wyprowadził jak owce i wiódł ich po pustyni jak stado.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
Prowadził ich bezpiecznie, tak że się nie lękali, a ich wrogów przykryło morze;
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
I przyprowadził ich do swej świętej granicy; do góry, którą nabyła jego prawica.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
Wypędził przed nimi narody, sznurem wyznaczył im dziedzictwo, żeby pokolenia Izraela mieszkały w swoich namiotach.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Oni jednak wystawiali na próbę i pobudzali do gniewu Boga Najwyższego, i nie strzegli jego świadectw.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Lecz odwrócili się i postępowali przewrotnie jak ich ojcowie, schodzili z drogi jak łuk zawodny.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Pobudzali go bowiem do gniewu przez swe wyżyny i rzeźbionymi posągami wzbudzali jego zazdrość.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
Gdy Bóg [to] usłyszał, rozgniewał się i wielce wzgardził Izraelem.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
I opuścił przybytek w Szilo; namiot, [który] rozbił wśród ludzi;
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
I oddał w niewolę swoją moc i swoją chwałę w ręce wroga.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
Wydał swój lud pod miecz i rozgniewał się na swoje dziedzictwo.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Ich młodzieńców pochłonął ogień, a ich dziewic nie wydano za mąż.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Ich kapłani padli od miecza, a ich wdowy nie lamentowały.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Lecz potem Pan ocknął się jak ze snu, jak mocarz wykrzykujący od wina.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
I uderzył na tyły swoich wrogów, okrył ich wieczną hańbą.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Ale choć wzgardził namiotem Józefa i pokolenia Efraima nie wybrał;
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
Jednak wybrał pokolenie Judy, górę Syjon, którą umiłował.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
I zbudował swoją świątynię jak wysoki [pałac]; jak ziemię, którą ugruntował na wieki.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
Wybrał też Dawida, swego sługę; wziął go z owczych zagród;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
Przywołał go, gdy chodził za karmiącymi [owcami], aby pasł Jakuba, jego lud, i Izraela, jego dziedzictwo.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
A on ich pasł w prawości swego serca i prowadził ich roztropną ręką.

< Masalimo 78 >