< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
قصیده آساف ای قوم من شریعت مرا بشنوید! گوشهای خود را به سخنان دهانم فراگیرید!۱
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
دهان خود را به مثل باز خواهم کرد به چیزهایی که از بنای عالم مخفی بود تنطق خواهم نمود.۲
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
که آنها را شنیده و دانسته‌ایم و پدران مابرای ما بیان کرده‌اند.۳
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
از فرزندان ایشان آنها راپنهان نخواهیم کرد. تسبیحات خداوند را برای نسل آینده بیان می‌کنیم و قوت او و اعمال عجیبی را که او کرده است.۴
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
زیرا که شهادتی دریعقوب برپا داشت و شریعتی در اسرائیل قرار دادو پدران ما را امر فرمود که آنها را به فرزندان خودتعلیم دهند؛۵
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
تا نسل آینده آنها را بدانند وفرزندانی که می‌بایست مولود شوند تا ایشان برخیزند و آنها را به فرزندان خود بیان نمایند؛۶
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
و ایشان به خدا توکل نمایند و اعمال خدا رافراموش نکنند بلکه احکام او را نگاه دارند.۷
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
ومثل پدران خود نسلی گردن کش و فتنه انگیزنشوند، نسلی که دل خود را راست نساختند وروح ایشان بسوی خدا امین نبود.۸
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
بنی افرایم که مسلح و کمان کش بودند، درروز جنگ رو برتافتند.۹
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
عهد خدا را نگاه نداشتند و از سلوک به شریعت او ابا نمودند،۱۰
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
واعمال و عجایب او را فراموش کردند که آنها رابدیشان ظاهر کرده بود،۱۱
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
و در نظر پدران ایشان اعمال عجیب کرده بود، در زمین مصر و در دیارصوعن.۱۲
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
دریا را منشق ساخته، ایشان را عبورداد و آبها را مثل توده برپا نمود.۱۳
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
و ایشان را درروز به ابر راهنمایی کرد و تمامی شب به نورآتش.۱۴
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
در صحرا صخره‌ها را بشکافت و ایشان را گویا از لجه های عظیم نوشانید.۱۵
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
پس سیلها رااز صخره بیرون آورد و آب را مثل نهرها جاری ساخت.۱۶
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
و بار دیگر بر او گناه ورزیدند و برحضرت اعلی در صحرا فتنه انگیختند،۱۷
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
و دردلهای خود خدا را امتحان کردند، چونکه برای شهوات خود غذا خواستند.۱۸
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
و بر‌ضد خداتکلم کرده، گفتند: «آیا خدا می‌تواند در صحراسفره‌ای حاضر کند؟۱۹
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
اینک صخره را زد و آبهاروان شد و وادیها جاری گشت. آیا می‌تواند نان رانیز بدهد. و گوشت را برای قوم خود حاضرسازد؟»۲۰
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
پس خدا این را شنیده، غضبناک شد و آتش در یعقوب افروخته گشت و خشم بر اسرائیل مشتعل گردید.۲۱
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
زیرا به خدا ایمان نیاوردند و به نجات او اعتماد ننمودند.۲۲
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
پس ابرها را از بالاامر فرمود و درهای آسمان را گشود۲۳
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
و من را برایشان بارانید تا بخورند و غله آسمان را بدیشان بخشید.۲۴
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
مردمان، نان زورآوران را خوردند وآذوقه‌ای برای ایشان فرستاد تا سیر شوند.۲۵
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
بادشرقی را در آسمان وزانید و به قوت خود، بادجنوبی را آورد،۲۶
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
و گوشت را برای ایشان مثل غبار بارانید و مرغان بالدار را مثل ریگ دریا.۲۷
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
وآن را در میان اردوی ایشان فرود آورد، گرداگردمسکن های ایشان.۲۸
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
پس خوردند و نیکو سیرشدند و موافق شهوات ایشان بدیشان داد.۲۹
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
ایشان از شهوت خود دست نکشیدند. و غذاهنوز در دهان ایشان بود۳۰
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
که غضب خدا برایشان افروخته شده؛ تنومندان ایشان را بکشت وجوانان اسرائیل را هلاک ساخت.۳۱
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
با وجود این همه، باز گناه ورزیدند و به اعمال عجیب او ایمان نیاوردند.۳۲
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
بنابراین، روزهای ایشان را در بطالت تمام کرد و سالهای ایشان را درترس.۳۳
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
هنگامی که ایشان را کشت اورا طلبیدند و بازگشت کرده، درباره خدا تفحص نمودند،۳۴
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
و به یاد آوردند که خدا صخره ایشان، و خدای تعالی ولی ایشان است.۳۵
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
اما به دهان خود او را تملق نمودند و به زبان خویش به اودروغ گفتند.۳۶
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
زیرا که دل ایشان با او راست نبودو به عهد وی موتمن نبودند.۳۷
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
اما او به حسب رحمانیتش گناه ایشان راعفو نموده، ایشان را هلاک نساخت بلکه بارهاغضب خود را برگردانیده، تمامی خشم خویش را برنینگیخت.۳۸
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
و به یاد آورد که ایشان بشرند، بادی که می‌رود و بر نمی گردد.۳۹
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
چند مرتبه درصحرا بدو فتنه انگیختند و او را در بادیه رنجانیدند.۴۰
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
و برگشته، خدا را امتحان کردند وقدوس اسرائیل را اهانت نمودند،۴۱
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
و قوت او رابه‌خاطر نداشتند، روزی که ایشان را از دشمن رهانیده بود.۴۲
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
که چگونه آیات خود را در مصرظاهر ساخت و معجزات خود را در دیار صوعن.۴۳
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
و نهرهای ایشان را به خون مبدل نمود ورودهای ایشان را تا نتوانستند نوشید.۴۴
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
انواع پشه‌ها در میان ایشان فرستاد که ایشان را گزیدند وغوکهایی که ایشان را تباه نمودند؛۴۵
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
و محصول ایشان را به کرم صد پا سپرد و عمل ایشان را به ملخ داد.۴۶
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
تاکستان ایشان را به تگرگ خراب کردو درختان جمیز ایشان را به تگرگهای درشت.۴۷
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
بهایم ایشان را به تگرگ سپرد و مواشی ایشان را به شعله های برق.۴۸
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
و آتش خشم خود را برایشان فرستاد، غضب و غیظ و ضیق را، به فرستادن فرشتگان شریر.۴۹
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
و راهی برای غضب خود مهیا ساخته، جان ایشان را از موت نگاه نداشت، بلکه جان ایشان را به وبا تسلیم نمود.۵۰
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
و همه نخست زادگان مصر را کشت، اوایل قوت ایشان را در خیمه های حام.۵۱
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
و قوم خود را مثل گوسفندان کوچانید وایشان را در صحرا مثل گله راهنمایی نمود.۵۲
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
وایشان را در امنیت رهبری کرد تا نترسند و دریادشمنان ایشان را پوشانید.۵۳
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
و ایشان را به حدودمقدس خود آورد، بدین کوهی که به‌دست راست خود تحصیل کرده بود.۵۴
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
و امت‌ها را از حضورایشان راند و میراث را برای ایشان به ریسمان تقسیم کرد و اسباط اسرائیل را در خیمه های ایشان ساکن گردانید.۵۵
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
لیکن خدای تعالی را امتحان کرده، بدو فتنه انگیختند و شهادات او را نگاه نداشتند.۵۶
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
وبرگشته، مثل پدران خود خیانت ورزیدند و مثل کمان خطا کننده منحرف شدند.۵۷
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
و به مقامهای بلند خود خشم او را به هیجان آوردند و به بتهای خویش غیرت او را جنبش دادند.۵۸
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
چون خدااین را بشنید غضبناک گردید و اسرائیل را به شدت مکروه داشت.۵۹
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
پس مسکن شیلو را ترک نمود، آن خیمه‌ای را که در میان آدمیان برپاساخته بود،۶۰
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
و (تابوت ) قوت خود را به اسیری داد و جمال خویش را به‌دست دشمن سپرد،۶۱
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
وقوم خود را به شمشیر تسلیم نمود و با میراث خود غضبناک گردید.۶۲
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
جوانان ایشان را آتش سوزانید و برای دوشیزگان ایشان سرود نکاح نشد.۶۳
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
کاهنان ایشان به دم شمشیر افتادند وبیوه های ایشان نوحه گری ننمودند.۶۴
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
آنگاه خداوند مثل کسی‌که خوابیده بودبیدار شد، مثل جباری که از شراب می‌خروشد،۶۵
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
و دشمنان خود را به عقب زد و ایشان را عارابدی گردانید.۶۶
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
و خیمه یوسف را رد نموده، سبط افرایم را برنگزید.۶۷
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
لیکن سبط یهودا رابرگزید و این کوه صهیون را که دوست می‌داشت.۶۸
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
و قدس خود را مثل کوههای بلند بنا کرد، مثل جهان که آن را تا ابدالاباد بنیاد نهاد.۶۹
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
و بنده خود داود را برگزید و او را از آغلهای گوسفندان گرفت.۷۰
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
از عقب میشهای شیرده او را آورد تاقوم او یعقوب و میراث او اسرائیل را رعایت کند.۷۱
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
پس ایشان را به حسب کمال دل خود رعایت نمود و ایشان را به مهارت دستهای خویش هدایت کرد.۷۲

< Masalimo 78 >