< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
The lernyng of Asaph. Mi puple, perseyue ye my lawe; bowe youre eere in to the wordis of my mouth.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I schal opene my mouth in parablis; Y schal speke perfite resouns fro the bigynnyng.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Hou grete thingis han we herd, aud we han knowe tho; and oure fadris. telden to vs.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Tho ben not hid fro the sones of hem; in anothir generacioun. And thei telden the heriyngis of the Lord, and the vertues of hym; and hise merueilis, whyche he dide.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
And he reiside witnessyng in Jacob; and he settide lawe in Israel. Hou grete thingis comaundide he to oure fadris, to make tho knowun to her sones;
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
that another generacioun knowe. Sones, that schulen be born, and schulen rise vp; schulen telle out to her sones.
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
That thei sette her hope in God, and foryete not the werkis of God; and that thei seke hise comaundementis.
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
Lest thei be maad a schrewid generacioun; and terrynge to wraththe, as the fadris of hem. A generacioun that dresside not his herte; and his spirit was not bileued with God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The sones of Effraym, bendinge a bouwe and sendynge arowis; weren turned in the dai of batel.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
Thei kepten not the testament of God; and thei nolden go in his lawe.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
And thei foryaten hise benefices; and hise merueils, whiche he schewide to hem.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
He dide merueils bifore the fadris of hem in the loond of Egipt; in the feeld of Taphneos.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He brak the see, and ledde hem thorou; and he ordeynede the watris as in a bouge.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
And he ledde hem forth in a cloude of the dai; and al niyt in the liytnyng of fier.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He brak a stoon in deseert; and he yaf watir to hem as in a myche depthe.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
And he ledde watir out of the stoon; and he ledde forth watris as floodis.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
And thei `leiden to yit to do synne ayens hym; thei excitiden hiye God in to ire, in a place with out water.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
And thei temptiden God in her hertis; that thei axiden meetis to her lyues.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
And thei spaken yuel of God; thei seiden, Whether God may make redi a bord in desert?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
For he smoot a stoon, and watris flowiden; and streemys yeden out in aboundaunce. Whether also he may yyue breed; ether make redi a bord to his puple?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Therfor the Lord herde, and delaiede; and fier was kindelid in Jacob, and the ire of God stiede on Israel.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
For thei bileueden not in God; nether hopiden in his heelthe.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
And he comaundide to the cloudis aboue; and he openyde the yatis of heuene.
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
And he reynede to hem manna for to eete; and he yaf to hem breed of heuene.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Man eet the breed of aungels; he sent to hem meetis in aboundance.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He turnede ouere the south wynde fro heuene; and he brouyte in bi his vertu the weste wynde.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
And he reynede fleischis as dust on hem; and `he reinede volatils fethered, as the grauel of the see.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
And tho felden doun in the myddis of her castels; aboute the tabernaclis of hem.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
And thei eeten, and weren fillid greetli, and he brouyte her desire to hem;
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
thei weren not defraudid of her desier. Yit her metis weren in her mouth;
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
and the ire of God stiede on hem. And he killide the fatte men of hem; and he lettide the chosene men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
In alle these thingis thei synneden yit; and bileuede not in the merueils of God.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
And the daies of hem failiden in vanytee; and the yeeris of hem faileden with haste.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Whanne he killide hem, thei souyten hym; and turneden ayen, and eerli thei camen to hym.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
And thei bithouyten, that God is the helper of hem; and `the hiy God is the ayenbier of hem.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
And thei loueden hym in her mouth; and with her tunge thei lieden to hym.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
Forsothe the herte of hem was not riytful with hym; nethir thei weren had feithful in his testament.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he is merciful, and he schal be maad merciful to the synnes of hem; and he schal not destrie hem. And he dide greetli, to turne awei his yre; and he kyndelide not al his ire.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
And he bithouyte, that thei ben fleische; a spirit goynge, and not turnynge ayen.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Hou oft maden thei hym wrooth in desert; thei stireden hym in to ire in a place with out watir.
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
And thei weren turned, and temptiden God; and thei wraththiden the hooli of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Thei bithouyten not on his hond; in the dai in the which he ayen bouyte hem fro the hond of the trobler.
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
As he settide hise signes in Egipt; and hise grete wondris in the feeld of Taphneos.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
And he turnede the flodis of hem and the reynes of hem in to blood; that thei schulden not drynke.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sente a fleisch flie in to hem, and it eet hem; and he sente a paddok, and it loste hem.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
And he yaf the fruytis of hem to rust; and he yaf the trauels of hem to locustis.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
And he killide the vynes of hem bi hail; and the moore trees of hem bi a frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
And he bitook the beestis of hem to hail; and the possessioun of hem to fier.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He sente in to hem the ire of his indignacioun; indignacioun, and ire, and tribulacioun, sendingis in bi iuel aungels.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made weie to the path of his ire, and he sparide not fro the deth of her lyues; and he closide togidere in deth the beestis of hem.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
And he smoot al the first gendrid thing in the lond of Egipt; the first fruytis of alle the trauel of hem in the tabernaclis of Cham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
And he took awei his puple as scheep; and he ledde hem forth as a flok in desert.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
And he ledde hem forth in hope, and thei dredden not; and the see hilide the enemyes of hem.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
And he brouyte hem in to the hil of his halewyng; in to the hil which his riythond gat. And he castide out hethene men fro the face of hem; and bi lot he departide to hem the lond in a cord of delyng.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
And he made the lynagis of Israel to dwelle in the tabernaclis of hem.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
And thei temptiden, and wraththiden heiy God; and thei kepten not hise witnessyngis.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
And thei turneden awei hem silf, and thei kepten not couenaunt; as her fadris weren turned in to a schrewid bouwe.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Thei stiriden him in to ire in her litle hillis; and thei terriden hym to indignacioun of her grauen ymagis.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
God herde, and forsook; and brouyte to nouyt Israel greetli.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
And he puttide awei the tabernacle of Sylo; his tabernacle where he dwellide among men.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
And he bitook the vertu of hem in to caitiftee; and the fairnesse of hem in to the hondis of the enemye.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
And he closide togidere his puple in swerd; and he dispiside his erytage.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fier eet the yonge men of hem; and the virgyns of hem weren not biweilid.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
The prestis of hem fellen doun bi swerd; and the widewis of hem weren not biwept.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
And the Lord was reisid, as slepynge; as miyti greetli fillid of wiyn.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
And he smoot hise enemyes on the hynderere partis; he yaf to hem euerlastyng schenschipe.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
And he puttide awei the tabernacle of Joseph; and he chees not the lynage of Effraym.
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
But he chees the lynage of Juda; he chees the hil of Syon, which he louede.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
And he as an vnicorn bildide his hooli place; in the lond, which he foundide in to worldis.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
And he chees Dauid his seruaunt, and took hym vp fro the flockis of scheep; he took hym fro bihynde scheep with lambren.
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
To feed Jacob his seruaunt; and Israel his eritage.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
And he fedde hem in the innocens of his herte; and he ledde hem forth in the vndurstondyngis of his hondis.

< Masalimo 78 >