< Masalimo 75 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
Hvalimo te, Bože, hvalimo; blizu je ime tvoje. Za tebe kazuju èudesa tvoja.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
“Kad vidim da je vrijeme, sudiæu pravo.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
Njiha se zemlja sa svijema koji žive na njoj, ja utvrðujem stupove njezine.”
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Kažem hvališama: ne hvalite se, i bezakonicima: ne dižite roga.
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
Ne dižite u vis roga svojega, ne govorite tvrdoglavo.
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
Jer uzvišivanje ne dolazi ni od istoka ni od zapada ni od pustinje;
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
Nego je Bog sudija, jednoga ponižuje a drugoga uzvišuje.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
Jer je èaša u ruci Gospodu, vino vri, natoèio je punu, i razdaje iz nje. I talog æe njezin progutati, ispiæe svi bezbožnici na zemlji.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
A ja æu kazivati dovijeka, pjevaæu Bogu Jakovljevu.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
“Sve æu rogove bezbožnicima polomiti, a rogovi pravednikovi uzvisiæe se.”

< Masalimo 75 >