< Masalimo 68 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
Przewodnikowi chóru. Psalm i pieśń Dawida. Niech Bóg powstanie, a rozproszeni będą jego wrogowie; niech pouciekają przed jego obliczem ci, którzy go nienawidzą.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
Jak dym jest rozwiany, tak [ich] rozpędzisz; jak wosk się rozpływa od ognia, [tak] niegodziwi poginą przed obliczem Boga.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
A sprawiedliwi będą się weselić i cieszyć przed obliczem Boga, i będą się radować niezmiernie.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Śpiewajcie Bogu, śpiewajcie psalmy jego imieniu, wywyższajcie tego, który przemierza niebiosa; PAN to jego imię, radujcie się przed jego obliczem.
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
Ojcem dla sierot i sędzią dla wdów jest Bóg w swym świętym przybytku.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
Bóg samotnym daje dom, więźniów uwalnia z oków, ale oporni mieszkają w suchej ziemi.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
Boże, gdy wyruszałeś przed swoim ludem, gdy kroczyłeś przez pustynię. (Sela)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
Ziemia się trzęsła, a niebiosa rozpływały się przed obliczem Boga i sama góra Synaj [zadrżała] przed obliczem Boga, Boga Izraela.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
Zesłałeś obfity deszcz, Boże, otrzeźwiłeś swoje dziedzictwo, gdy omdlewało.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Twoje zastępy mieszkają w nim; ty, Boże, w swojej dobroci przygotowałeś [je] dla ubogiego.
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
Pan dał [swoje] słowo, wielki był zastęp zwiastujących dobre wieści.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
Królowie wojsk uciekali, uciekali; a ta, która doglądała domu, dzieliła łupy.
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
Chociaż musieliście leżeć wśród kotłów, [będziecie] jak skrzydła gołębicy pokryte srebrem, a jej pióra żółtym złotem.
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
Gdy Wszechmogący rozproszył królów w ziemi, była biała jak śnieg na [górze] Salmon.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
Góra Boża jest jak góra Baszanu, wzgórze wysokie, jak góra Baszanu.
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Dlaczego wyskakujecie, wzgórza wysokie? Na tej górze spodobało się Bogu mieszkać, tam PAN będzie mieszkał na wieki.
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
Rydwanów Bożych [jest] dwadzieścia tysięcy, wiele tysięcy aniołów; Pan [przebywa] wśród nich w świątyni, [jak na] Synaju.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
Wstąpiłeś na wysokość, poprowadziłeś pojmanych jeńców, przyjąłeś dary dla ludzi, nawet dla buntowników, aby PAN Bóg mógł [z nimi] zamieszkać.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Błogosławiony Pan; codziennie obsypuje nas [swymi dobrami] Bóg naszego zbawienia. (Sela)
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
Nasz Bóg jest Bogiem zbawienia, Pan BÓG wybawia od śmierci.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
Bóg zrani głowę swoich wrogów i owłosioną czaszkę tego, który trwa w swoich grzechach.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
Pan powiedział: Wyprowadzę znów [swoich] z Baszanu, wyprowadzę [ich] znowu z głębin morskich;
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
Aby twoja stopa była skąpana we krwi, a język twoich psów [we krwi] wrogów.
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
Widzieli twoje pochody, Boże; pochody mego Boga, mego Króla w świątyni.
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
Przodem szli śpiewacy, za nimi grający na instrumentach, wśród nich dziewczęta uderzające w bębenki.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
W zgromadzeniach błogosławcie Boga, Pana, wy, którzy pochodzicie ze źródła Izraela.
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
Tam [jest] mały Beniamin, który im przewodzi, władcy Judy i ich hufce, władcy Zebulona i władcy Neftalego.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
Twój Bóg obdarzył cię siłą; umocnij, Boże, to, co dla nas uczyniłeś.
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
Ze względu na twoją świątynię w Jeruzalem królowie będą przynosić ci dary.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Zgrom rzeszę kopijników, stado byków z cielcami ludu, chlubiących się kawałkiem srebra; rozprosz narody pragnące wojny.
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
Przyjdą dostojnicy z Egiptu; Etiopia szybko wyciągnie swe ręce do Boga.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
Śpiewajcie Bogu, królestwa ziemi, wysławiajcie Pana. (Sela)
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
Temu, który przemierza najwyższe niebiosa odwieczne; oto wydaje swój głos, głos potężny.
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Uznajcie moc Boga, jego majestat [jest] nad Izraelem i jego moc w obłokach.
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
Groźny jesteś, Boże, ze swych świętych przybytków; Bóg Izraela sam daje moc i siłę [swemu] ludowi. [Niech będzie] Bóg błogosławiony.

< Masalimo 68 >