< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Ta, u Boga je mir duši mojoj, od njega je spasenje moje!
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Ta, on je grad moj i spasenje moje, utoèište moje, neæu posrnuti nimalo.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Dokle æete napadati na èovjeka? Svi hoæete da ga oborite kao zid navaljen, kao ogradu isprovaljivanu.
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Baš naumiše da ga svrgnu s visine, omilje im laž, ustima blagosiljaju a u srcu kunu.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Da, u Bogu se smiri, dušo moja; jer je u njemu nad moj.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
On je grad moj i spasenje moje, utoèište moje, neæu posrnuti.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
U Bogu je spasenje moje i slava moja, tvrdi grad i pristanište meni je u Bogu.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Narode! uzdaj se u njega u svako doba; izlivajte pred njim srce svoje; Bog je naše utoèište.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Ta, sinovi su prostaèki ništa, sinovi su gospodski laž, da se metnu na mjerila, bili bi lakši nego ništa.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ne uzdajte se u vlast ni u otimanje, nemojte biti ništavi; kad raste bogatstvo, ne dajte da vam srce prione za nj.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Jednom reèe Bog i više puta èuh, da je krjepost u Boga.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
I u tebe je, Gospode, milost; jer ti plaæaš svakome po djelima njegovijem.

< Masalimo 62 >