< Masalimo 61 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
Èuj, Bože, viku moju, slušaj molitvu moju.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Od kraja zemlje vièem k tebi, kad klonu srce moje. Izvedi me na goru, gdje se ne mogu popeti.
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
Jer si ti utoèište moje, tvrdi zaklon od neprijatelja.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Da živim u stanu tvom dovijeka, i poèinem pod krovom krila tvojih.
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Jer ti, Bože, èuješ zavjete moje i daješ mi dostojanje onijeh koji poštuju ime tvoje.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Dodaj dane k danima carevijem, i godine njegove produlji od koljena na koljeno.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
Neka caruje dovijeka pred Bogom; zapovjedi milosti i istini neka ga èuvaju.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Tako æu pjevati imenu tvojemu svagda, izvršujuæi zavjete svoje svaki dan.

< Masalimo 61 >