< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
For the End, a Psalm of David amongst the Hymns for the eighth. O Lord, rebuke me not in your wrath, neither chasten me in your anger.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Pity me, O Lord; for I am weak: heal me, O Lord; for my bones are vexed.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
My soul also is grievously vexed: but you, O Lord, how long?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return, O Lord, deliver my soul: save me for your mercy's sake.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For in death no man remembers you: and who will give you thanks in Hades? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I am wearied with my groaning; I shall wash my bed every night; I shall water my couch with tears.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mine eye is troubled because of my wrath; I am worn out because of all my enemies.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Depart from me, all you that work iniquity; for the Lord has heard the voice of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
The Lord has listened to my petition; the Lord has accepted my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Let all mine enemies be put to shame and sore troubled: let them be turned back and grievously put to shame speedily.

< Masalimo 6 >