< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
`In Ebreu thus, To the victorie, lese thou not the semeli song, `ether the `swete song of Dauid, `whanne he fledde fro the face of Saul in to the denne. `In Jeroms translacioun thus, For victorie, that thou lese not Dauid, meke and simple, whanne he fledde fro the face of Saul in to the denne. God, haue thou merci on me, haue thou merci on me; for my soule tristith in thee. And Y schal hope in the schadewe of thi wyngis; til wickidnesse passe.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
I schal crye to God altherhiyeste; to God that dide wel to me.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
He sente fro heuene, and delyuerede me; he yaf in to schenschip hem that defoulen me. God sente his merci and his treuthe,
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
and delyuerede my soule fro the myddis of whelpis of liouns; Y slepte disturblid. The sones of men, the teeth of hem ben armuris and arowis; and her tunge is a scharp swerd.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
God, be thou enhaunsid aboue heuenes; and thi glorie aboue al erthe.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Thei maden redi a snare to my feet; and thei greetly boweden my lijf. Thei delueden a diche bifore my face; and thei felden doun in to it.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
God, myn herte is redi, myn herte is redi; Y schal singe, and Y schal seie salm.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Mi glorie, rise thou vp; sautrie and harpe, rise thou vp; Y schal rise vp eerli.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Lord, Y schal knouleche to thee among puplis; and Y schal seie salm among hethene men.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
For thi merci is magnified til to heuenes; and thi treuthe til to cloudis.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
God, be thou enhaunsid aboue heuenes; and thi glorie ouer al erthe.

< Masalimo 57 >