< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
Smiluj se na me, Bože, jer èovjek hoæe da me proguta, neprijatelj me svaki dan pritješnjuje.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Neprijatelji moji svaki dan traže da me progutaju; jer mnogi napadaju na me oholo.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Kad me je strah, ja se u tebe uzdam.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
Bogom se hvalim za rijeè njegovu; u Boga se uzdam, ne bojim se; šta æe mi uèiniti tijelo?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Svaki dan izvræu rijeèi moje; što god misle, sve meni o zlu.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
Skupljaju se, prikrivaju se, paze za petama mojima; jer traže dušu moju.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Kod ovake zloæe izbavi od njih, u gnjevu obori narode, Bože.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
U tebe je izbrojeno moje potucanje, suze se moje èuvaju u sudu kod tebe, one su u knjizi tvojoj.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Neprijatelji moji ustupaju natrag, kad tebe prizivljem; po tom znam da je Bog sa mnom.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
Bogom se hvalim za rijeè njegovu, Gospodom se hvalim za rijeè njegovu.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
U Boga se uzdam, ne bojim se; šta æe mi uèiniti èovjek?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Tebi sam se, Bože, zavjetovao; tebe æu hvaliti;
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Jer si izbavio dušu moju od smrti, noge moje od spoticanja, da bih hodio pred licem Božjim, u svjetlosti živijeh.

< Masalimo 56 >