< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
For the end, concerning the people that were removed from the sanctuary, by David for a memorial, when the Philistines caught him in Geth. Have mercy upon me, O God; for man has trodden me down; all the day long he warring has afflicted me.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Mine enemies have trodden me down all the day from the dawning of the day; for there are many warring against me.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
They shall be afraid, but I will trust in you.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
In God I will praise my words; all the day have I hoped in God; I will not fear what flesh shall do to me.
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
All the day long they have abominated my words; all their devices [are] against me for evil.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
They will dwell near and hide [themselves]; they will watch my steps, accordingly as I have waited patiently in my soul.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
You will on no account save them; you will bring down the people in wrath.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
O God, I have declared my life to you; you has set my tears before you, even according to your promise.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Mine enemies shall be turned back, in the day wherein I shall call upon you; behold, I know that you are my God.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
In God, will I praise [his] word; in the Lord will I praise [his] saying.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
I have hoped in God; I will not be afraid of what man shall do to me.
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
The vows of your praise, O God, which I will pay, are upon me.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
For you have delivered my soul from death, and my feet from sliding, that I should be well-pleasing before God in the land of the living.

< Masalimo 56 >