< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
For the end, amongst Hymns of instruction by David. Listen, O God, to my prayer; and disregard not my supplication.
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
Attend to me, and listen to me: I was grieved in my (meditation) and troubled;
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
because of the voice of the enemy, and because of the oppression of the sinner: for they brought iniquity against me, and were wrathfully angry with me.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
My heart was troubled within me; and the fear of death fell upon me.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
Fear and trembling came upon me, and darkness covered me.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
And I said, O that I had wings as [those] of a dove! then would I flee away, and be at rest.
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
Behold! I have fled afar off, and lodged in the wilderness. (Pause)
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
I waited for him that should deliver me from distress of spirit and tempest.
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
Destroy, O Lord, and divide their tongues: for I have seen iniquity and gain saying in the city.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
Day and night he shall go round about it upon its walls: iniquity and sorrow and unrighteousness [are] in the midst of it;
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
and usury and craft have not failed from its streets.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
For if an enemy had reproached me, I would have endured it; and if one who hated [me] had spoken vauntingly against me, I would have hid myself from him.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
But you, O man like minded, my guide, and my acquaintance,
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
who in companionship with me sweetened [our] food: we walked in the house of God in concord.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
Let death come upon them, and let them go down alive into Hades, for iniquity is in their dwellings, in the midst of them. (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
I cried to God, and the Lord listened to me.
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
Evening, and morning, and at noon I will declare and make known [my wants]: and he shall hear my voice.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
He shall deliver my soul in peace from them that draw near to me: for they were with me in many [cases].
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
God shall hear, and bring them low, [even] he that has existed from eternity. (Pause) For they suffer no reverse, and [therefore] they have not feared God.
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
He has reached forth his hand for retribution; they have profaned his covenant.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
They were scattered at the anger of his countenance, and his heart drew near them. His words were smoother than oil, yet are they darts.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
Cast your care upon the Lord, and he shall sustain you; he shall never suffer the righteous to be moved.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
But you, O God, shall bring them down to the pit of destruction; bloody and crafty men shall not live out half their days; but I will hope in you, O Lord.

< Masalimo 55 >