< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
The salm of Asaph. God, the Lord of goddis, spak; and clepide the erthe,
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
fro the risynge of the sunne til to the goyng doun. The schap of his fairnesse fro Syon,
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
God schal come opynli; oure God, and he schal not be stille. Fier schal brenne an hiye in his siyt; and a strong tempest in his cumpas.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
He clepide heuene aboue; and the erthe, to deme his puple.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Gadere ye to hym hise seyntis; that ordeynen his testament aboue sacrifices.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
`And heuenes schulen schewe his riytfulnesse; for God is the iuge.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Mi puple, here thou, and Y schal speke to Israel; and Y schal witnesse to thee, Y am God, thi God.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
I schal not repreue thee in thi sacrifices; and thi brent sacrifices ben euere bifor me.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
I schal not take calues of thin hows; nethir geet buckis of thi flockis.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
For alle the wyelde beestis of wodis ben myne; werk beestis, and oxis in hillis.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
I haue knowe alle the volatils of heuene; and the fairnesse of the feeld is with me.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
If Y schal be hungry, Y schal not seie to thee; for the world and the fulnesse therof is myn.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Whether Y schal eete the fleischis of boolis? ethir schal Y drynke the blood of geet buckis?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Offre thou to God the sacrifice of heriyng; and yelde thin avowis to the hiyeste God.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
And inwardli clepe thou me in the dai of tribulacioun; and Y schal delyuere thee, and thou schalt onoure me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
But God seide to the synnere, Whi tellist thou out my riytfulnessis; and takist my testament bi thi mouth?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Sotheli thou hatidist lore; and hast cast awey my wordis bihynde.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
If thou siyest a theef, thou `hast runne with hym; and thou settidist thi part with avowtreris.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Thi mouth was plenteuouse of malice; and thi tunge medlide togidere giles.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Thou sittynge spakist ayens thi brother, and thou settidist sclaundir ayens the sone of thi modir;
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
thou didist these thingis, and Y was stille. Thou gessidist wickidli, that Y schal be lijk thee; Y schal repreue thee, and Y schal sette ayens thi face.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Ye that foryeten God, vndurstonde these thingis; lest sum tyme he rauysche, and noon be that schal delyuere.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
The sacrifice of heriyng schal onoure me; and there is the weie, where ynne Y schal schewe to hym the helthe of God.

< Masalimo 50 >