< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Pieśń i psalm dla synów Korego. Wielki jest PAN i godzien wielkiej chwały w mieście naszego Boga, na swej świętej górze.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Pięknie wzniesiona, radością całej ziemi [jest] góra Syjon na krańcach północy, miasto wielkiego Króla.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
Bóg w pałacach jego jest uznany za twierdzę.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
Bo oto zgromadzili się królowie i razem ruszyli.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
Gdy zobaczyli, zdumieli się, przerazili się i uciekli.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Strach ich tam ogarnął i ból, jak rodzącą kobietę.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
Wiatrem wschodnim rozbijasz okręty Tarszisz.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
To, co słyszeliśmy, [to] zobaczyliśmy w mieście PANA zastępów, w mieście naszego Boga; Bóg je ugruntuje na wieki. (Sela)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
Rozważamy, o Boże, twoje miłosierdzie we wnętrzu twej świątyni.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
Jak twoje imię, Boże, tak i chwała twoja [sięga] aż po krańce ziemi; twoja prawica pełna jest sprawiedliwości.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Niech się weseli góra Syjon, niech się radują córki Judy z powodu twoich sądów.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Okrążcie Syjon i obejdźcie go, policzcie jego wieże.
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
Przyjrzyjcie się jego wałom obronnym, oglądajcie jego pałace, abyście mogli opowiadać przyszłemu pokoleniu.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
Bo ten Bóg jest naszym Bogiem na wieki wieków, on będzie nas prowadził aż do śmierci.

< Masalimo 48 >