< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
Svi narodi, zaplještite rukama, pokliknite Bogu glasom radosnijem.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
Jer je višnji Gospod strašan, car veliki nad svom zemljom.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
Pokori nam narode i plemena pod noge naše.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
Izbra nam dostojanje naše, krasotu Jakova, koji mu omilje.
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
Ide Bog uz podvikivanje, Gospod uz glas trubni.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Pojte Bogu, pojte; pojte caru našemu, pojte;
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
Jer je Bog car od sve zemlje, pojte pjesmu.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
Bog caruje nad narodima; Bog sjedi na svetom prijestolu svom.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
Knezovi narodni sastavljaju se s narodom Boga Avramova. Jer su štitovi zemaljski Božiji. Da je uzvišen!

< Masalimo 47 >