< Masalimo 47 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
To victorie, a salm to the sones of Chore. Alle ye folkis, make ioie with hondis; synge ye hertli to God in the vois of ful out ioiyng.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
For the Lord is hiy and ferdful; a greet kyng on al erthe.
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
He made puplis suget to vs; and hethene men vndur oure feet.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
He chees his eritage to vs; the fairnesse of Jacob, whom he louyde.
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
God stiede in hertli song; and the Lord in the vois of a trumpe.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
Synge ye to oure God, synge ye; synge ye to oure kyng, synge ye.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
For God is kyng of al erthe; synge ye wiseli.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
God schal regne on hethene men; God sittith on his hooli seete.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.
The princes of puplis ben gaderid togidere with God of Abraham; for the stronge goddis of erthe ben reisid greetli.

< Masalimo 47 >