< Masalimo 45 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Teèe iz srca mojega rijeè dobra; rekoh: djelo je moje za cara; jezik je moj trska hitroga pisara.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Ti si najljepši izmeðu sinova ljudskih, blagodat teèe iz usta tvojih, jer te je blagoslovio Bog dovijeka.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Pripaši, junaèe, uz bedru svoju maè svoj, èast svoju i krasotu svoju.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
I tako okiæen pohitaj, sjedi na kola za istinu i krotku pravdu, i desnica æe tvoja pokazati èudesa.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Oštre su strijele tvoje; narodi æe pasti pod vlast tvoju; prostrijeliæe srca neprijatelja carevijeh.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Prijesto je tvoj, Bože, vjeèan i nepokolebljiv; skiptar je carstva tvojega skiptar pravice.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Ljubiš pravdu i mrziš na bezakonje; toga radi pomaza te, Bože, Bog tvoj uljem radosti više nego drugove tvoje.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Sve haljine tvoje mirišu smirnom, alojem i kasijom. Koji žive u dvorima od Minijske slonove kosti, oni te vesele.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Carske kæeri dvore te; s desne ti strane stoji carica u Ofirskom zlatu.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Èuj, kæeri, pogledaj i obrati k meni uho svoje, zaboravi narod svoj i dom oca svojega.
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
I caru æe omiljeti ljepota tvoja; jer je on Gospod tvoj, i njemu se pokloni.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
Kæi Tirova doæi æe s darovima, najbogatiji u narodu tebe æe moliti.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Sva je ukrašena kæi careva iznutra, haljina joj je zlatom iskiæena.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
U vezenoj haljini vode je k caru; za njom vode k tebi djevojke, druge njezine.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Vode ih veselo i radosno, ulaze u dvor carev.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Mjesto otaca tvojih biæe sinovi tvoji, postaviæeš ih knezovima po svoj zemlji.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Uèiniæu da se ne zaboravlja ime tvoje od koljena na koljeno; po tom æe te slaviti narodi vavijek vijeka.

< Masalimo 45 >