< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
Salmo de David, para recordar. JEHOVÁ, no me reprendas en tu furor, ni me castigues en tu ira.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
Porque tus saetas descendieron á mí, y sobre mí ha caído tu mano.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
No hay sanidad en mi carne á causa de tu ira; ni hay paz en mis huesos á causa de mi pecado.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
Porque mis iniquidades han pasado mi cabeza: como carga pesada se han agravado sobre mí.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
Pudriéronse, corrompiéronse mis llagas, á causa de mi locura.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
Estoy encorvado, estoy humillado en gran manera, ando enlutado todo el día.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
Porque mis lomos están llenos de irritación, y no hay sanidad en mi carne.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
Estoy debilitado y molido en gran manera; bramo á causa de la conmoción de mi corazón.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Señor, delante de ti están todos mis deseos; y mi suspiro no te es oculto.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
Mi corazón está acongojado, hame dejado mi vigor; y aun la misma luz de mis ojos no está conmigo.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Mis amigos y mis compañeros se quitaron de delante de mi plaga; y mis cercanos se pusieron lejos.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Y los que buscaban mi alma armaron lazos; y los que procuraban mi mal hablaban iniquidades, y meditaban fraudes todo el día.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
Mas yo, como [si fuera] sordo, no oía; [y estaba] como un mudo, [que] no abre su boca.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Fuí pues como un hombre que no oye, y que en su boca no tiene reprensiones.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
Porque á ti, oh Jehová, esperé yo: tú responderás, Jehová Dios mío.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
Porque dije: Que no se alegren de mí: cuando mi pie resbalaba, sobre mí se engrandecían.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
Empero yo estoy á pique de claudicar, y mi dolor está delante de mí continuamente.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
Por tanto denunciaré mi maldad; congojaréme por mi pecado.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
Porque mis enemigos están vivos [y] fuertes: y hanse aumentado los que me aborrecen sin causa:
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
Y pagando mal por bien me son contrarios, por seguir yo lo bueno.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
No me desampares, oh Jehová: Dios mío, no te alejes de mí.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Apresúrate á ayudarme, oh Señor, mi salud.

< Masalimo 38 >