< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Veselite se pravednici pred Gospodom; pravednima dolikuje slaviti.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Slavite Gospoda guslama, udarajte mu u psaltir od deset žica.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Pjevajte mu pjesmu novu, složno udarajte podvikujuæi;
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Jer je prava rijeè Gospodnja, i svako djelo njegovo istinito.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
On ljubi pravdu i sud, dobrote je Gospodnje puna zemlja.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Rijeèju Gospodnjom nebesa se stvoriše, i duhom usta njegovijeh sva vojska njihova.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Kao u gomilu sabra vodu morsku, i propasti metnu u spreme.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Nek se boji Gospoda sva zemlja, i neka strepi pred njim sve što živi po vasiljenoj;
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Jer on reèe, i postade; on zapovjedi, i pokaza se.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Gospod razbija namjere neznabošcima, uništava pomisli narodima.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Namjera je Gospodnja tvrda dovijeka, misli srca njegova od koljena na koljeno.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Blago narodu, kojemu je Bog Gospod, plemenu, koje je on izabrao sebi za naslijeðe.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
S neba gleda Gospod, vidi sve sinove ljudske;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
S prijestola, na kome sjedi, pogleda na sve koji žive na zemlji.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
On je stvorio sva srca njihova, on i zna sva djela njihova.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Neæe pomoæi caru velika (sila) neæe zaštititi jakoga velika snaga;
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Nije u konju uzdanje da æe pomoæi; ako mu je i velika snaga, neæe izbaviti.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Gle, oko je Gospodnje na onima koji ga se boje, i na onima koji èekaju milost njegovu.
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
On æe dušu njihovu izbaviti od smrti, i prehraniti ih u gladne godine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Duša se naša uzda u Gospoda; on je pomoæ naša i štit naš.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
O njemu se veseli srce naše; jer se u sveto ime njegovo uzdamo.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Da bude milost tvoja, Gospode, na nama, kao što se uzdamo u tebe.

< Masalimo 33 >